< Masalimo 8 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
Unto the end, for the presses: a psalm of David. O Lord our Lord, how admirable is thy name in the whole earth! For thy magnificence is elevated above the heavens.
2 Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
Out of the mouth of infants and of sucklings thou hast perfected praise, because of thy enemies, that thou mayst destroy the enemy and the avenger.
3 Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
For I will behold thy heavens, the works of thy fingers: the moon and the stars which thou hast founded.
4 munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
What is man that thou art mindful of him? or the son of man that thou visitest hi?
5 Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
Thou hast made him a little less than the angels, thou hast crowned him with glory and honour:
6 Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
And hast set him over the works of thy hands.
7 nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
Thou hast subjected all things under his feet, all sheep and oxen: moreover the beasts also of the fields.
8 mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
The birds of the air, and the fishes of the sea, that pass through the paths of the sea.
9 Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!
O Lord our Lord, how admirable is thy name in all the earth!

< Masalimo 8 >