< Masalimo 79 >
1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Псалом Асафа. Боже! язычники пришли в наследие Твое, осквернили святый храм Твой, Иерусалим превратили в развалины;
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
трупы рабов Твоих отдали на съедение птицам небесным, тела святых Твоих - зверям земным;
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
пролили кровь их, как воду, вокруг Иерусалима, и некому было похоронить их.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
Мы сделались посмешищем у соседей наших, поруганием и посрамлением у окружающих нас.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Доколе, Господи, будешь гневаться непрестанно, будет пылать ревность Твоя, как огонь?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Пролей гнев Твой на народы, которые не знают Тебя, и на царства, которые имени Твоего не призывают,
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
ибо они пожрали Иакова и жилище его опустошили.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Не помяни нам грехов наших предков; скоро да предварят нас щедроты Твои, ибо мы весьма истощены.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Помоги нам, Боже, Спаситель наш, ради славы имени Твоего; избавь нас и прости нам грехи наши ради имени Твоего.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Для чего язычникам говорить: “где Бог их?” Да сделается известным между язычниками пред глазами нашими отмщение за пролитую кровь рабов Твоих.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Да придет пред лице Твое стенание узника; могуществом мышцы Твоей сохрани обреченных на смерть.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
Семикратно возврати соседям нашим в недро их поношение, которым они Тебя, Господи, поносили.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
А мы, народ Твой и Твоей пажити овцы, вечно будем славить Тебя и в род и род возвещать хвалу Тебе.