< Masalimo 79 >
1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Psalm podany Asafowi. O Boże! wtargnęli poganie w dziedzictwo twoje, splugawili kościół twój święty, obrócili Jeruzalem w kupy gruzu.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
Dali trupy sług twoich na pokarm ptastwu powietrznemu, ciała świętych twoich bestyjom ziemskim.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
Wylali krew ich jako wodę około Jeruzalemu, a nie był, ktoby ich pochował.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
Staliśmy się pohańbieniem u sąsiadów naszych; śmiechowiskiem i igrzyskiem u tych, którzy są około nas.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Dokądże, o Panie? azaż na wieki gniewać się będziesz? a jako ogień pałać będzie zapalczywość twoja?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Wylij gniew twój na pogan, którzy cię nie znają, i na królestwa, które imienia twego nie wzywają.
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
Albowiemci pożarli Jakóba, a mieszkanie jego spustoszyli.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Nie wspominajże nam przeszłych nieprawości naszych; niech nas rychło uprzedzi miłosierdzie twoje, bośmy bardzo znędzeni.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Wspomóżże nas, o Boże zbawienia naszego! dla chwały imienia twego, a wyrwij nas, i bądź miłościw grzechom naszym dla imienia twego.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Przeczżeby mieli mówić poganie: Gdzież jest Bóg ich? Bądź znacznym między poganami, przed oczyma naszemi, dla pomsty krwi sług twoich, która jest wylana.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Niech przyjdzie przed oblicze twoje narzekanie więźniów, a według wielkości ramienia twego zachowaj ostatki tych, co są na śmierć skazani.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
A oddaj sąsiadom naszym siedmiorako na łono ich za pohańbienie ich, któreć uczynili, o Panie!
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
Ale my lud twój i owce pastwiska twego, będziemy cię wysławiali na wieki; od narodu do narodu będziemy opowiadać chwałę twoję.