< Masalimo 79 >

1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
Asaphin Psalmi. Jumala, pakanat ovat perikuntaas karanneet: he ovat saastuttaneet pyhän temppelis, ja Jerusalemista kiviraunion tehneet.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
He antoivat sinun palveliais ruumiit linnuille taivaan alla ruaksi, ja pyhäis lihan maan pedoille.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
He vuodattivat heidän verensä niinkuin veden Jerusalemin ympärille, ja ei kenkään haudannut.
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
Me olemme läsnäasuvaisillemme nauruksi tulleet, häväistykseksi ja pilkaksi niille, jotka meidän ympärillämme ovat.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
Herra, kuinka kauvan sinä taukoomata niin vihainen olet? ja annat kiivautes palaa niinkuin tulen?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Vuodata vihas pakanain päälle, jotka ei sinua tunne, ja niiden valtakuntain päälle, jotka ei sinun nimeäs avuksi huuda;
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
Sillä he ovat Jakobin syöneet, ja hänen huoneensa hävittäneet.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Älä muistele meidän entisiä pahoja tekojamme: armahda sinuas nopiasti meidän päällemme; sillä me olemme sangen viheliäisiksi tulleet.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Auta meitä, meidän autuutemme Jumala, sinun nimes kunnian tähden: pelasta meitä, ja anna meille synnit anteeksi sinun nimes tähden.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Miksis sallit pakanain sanoa: kussa on nyt heidän Jumalansa? ilmoitettakaan pakanain seassa, meidän silmäimme edessä, sinun palveliais veren kosto, joka vuodatettu on!
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Anna etees tulla vankein huokaukset: suuren käsivartes kautta, korjaa kuoleman lapset,
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
Ja kosta meidän läsnäasuvaisillemme seitsemin kerroin heidän helmaansa heidän pilkkansa, jolla he sinua, Herra, pilkanneet ovat.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
Mutta me sinun kansas, ja sinun laitumes lauma, kiitämme sinua ijankaikkisesti, ja julistamme sinun kiitostas suvusta sukuun.

< Masalimo 79 >