< Masalimo 79 >
1 Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
A Psalm for Asaph. O God, the heathen are come into your inheritance; they have polluted your holy temple; they have made Jerusalem a storehouse of fruits.
2 Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
They have given the dead bodies of your servants [to be] food for the birds of the sky, the flesh of your holy ones for the wild beasts of the earth.
3 Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
They have shed their blood as water, round about Jerusalem; and there was none to bury [them].
4 Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
We are become a reproach to our neighbors, a scorn and derision to them [that are] round about us.
5 Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
How long, O Lord? will you be angry for ever? shall your jealousy burn like fire?
6 Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
Pour out your wrath upon the heathen that have not known you, and upon the kingdoms which have not called upon your name.
7 pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
For they have devoured Jacob, and laid his place waste.
8 Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
Remember not our old transgressions; let your tender mercies speedily prevent us; for we are greatly impoverished.
9 Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
Help us, O God our Saviour; for the glory of your name, O Lord, deliver us; and be merciful to our sins, for your name's sake.
10 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
Lets haply they should say among the heathen, Where is their God? and let the avenging of your servant's blood that has been shed be known among the heathen before our eyes.
11 Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
Let the groaning of the prisoners come in before you; according to the greatness of your arm preserve the sons of the slain ones.
12 Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
Repay to our neighbors sevenfold into their bosom their reproach, with which they have reproached you, O Lord.
13 Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.
For we are your people and the sheep of your pasture; we will give you thanks for ever; we will declare your praise throughout all generations.