< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Pesem ukovita Asafova. Poslušaj, ljudstvo moje, nauk moj; nagnite uho svoje govoru mojih ust.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
V priliki odprem usta svoja; od sebe dam skrivnosti časov nekdanjih,
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Kar smo slišali in znali, ko so nam pravili pradedje naši.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Prikrivali ne bodemo njih otrokom, naslednjemu rodu, da oznanjajo hvalo Gospodovo in moč njegovo, in čudovita dela njegova, katera je storil.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
Ker ustanovil je pričanje v Jakobu in postavil zakon v Izraelu, ko je zapovedal pradedom našim, oznanjati svojim otrokom.
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Da vedó, naslednji rod, otroci prihodnji, in vstanejo ter oznanjajo otrokom svojim.
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
Upanje svoje naj stavijo v Boga, in ne pozabijo naj dejanj Boga mogočnega, temuč hranijo naj zapovedi njegove.
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
In ne bodejo naj kakor njih pradedje, rod trdovraten in uporen; rod, kateri ni popravil srca svojega, in katerega duh ni bil stanoviten proti Bogu mogočnemu,
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Kakor nasledniki Efrajmovi, kateri oboroženi streljajo z lokom in hrbte obračajo ob času bitve.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
Ohranili niso zaveze Božje, in branili so se hoditi po zakonu njegovem,
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
Pozabivši dejanj njegovih, in čudovitih del njegovih, katera jim je bil pokazal.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Pred pradedi njihovimi je delal čuda, v deželi Egiptovski, na polji Taniškem.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Razklal je bil morje, da jih je prepeljal čez, in postavil je vode, kakor kùp.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
In spremljal jih je z oblakom podnevi, in vso noč sè svetlim ognjem.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
Razklal je bil skale v puščavi, da bi pijačo pripravil v valovih preobilo.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
Valove je izpeljal iz skale, in vode dol spuščal kakor reke.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Vendar so dalje grešili še zoper njega, in dražili Najvišjega v sami suhi deželi.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
In izkušajoč Boga mogočnega v srci svojem, térjali so jedi po svojega srca želji.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
In grdo govoreč zoper Boga, rekli so: "Ali bi mogel Bog mogočni napraviti mizo v tej puščavi?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Glej, tako je udaril skalo, da so tekle vode, in potoki so se udrli, ali bi mogel dati tudi živeža? ali bi pripravil mesa svojemu ljudstvu?"
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Zato je Gospod slišal in se razjaril; in ogenj se je bil vnel zoper Jakoba, in jeza je tudi gorela zoper Izraela.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Ker niso verovali v Boga, in niso zaupali v blaginjo njegovo.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Dasi je bil zapovedal gornjim oblakom zgoraj in odprl vrata nebeška,
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
In dežil nad nje máno za jed in dajal žito nebeško;
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Kruh najmočnejših je jedel vsak; popotnico jim je pošiljal do sitega.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Zagnal je sever na nebesih, in z močjo svojo pripeljal jug.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Ko je dežil nad nje meso kakor prah, in kakor morski pések tiče krilate;
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
Metal jih je med šatore, okolo prebivališč svojih.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
In jedli so in bili so nasiteni močno, in česar so poželeli, prinesel jim je.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
Še niso bili iznebili se poželenja svojega, še je bila jed njih v njihovih ustih;
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
Ko je jeza Božja goreča proti njim morila med najmočnejimi iz med njih in pokončavala mladeniče Izraelske.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Po vsem tem so še grešili in niso verovali zavoljo čudovitih dél njegovih.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Zatorej je pogubljal v ničemurnosti njih dní, in njih leta v strahu.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Ko jih je pobijal, ako so popraševali po njem in izpreobrnivši se zjutraj iskali Boga mogočnega,
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
Spomnivši se, da je bil Bog njih skala in Bog mogočni najvišji njih rešnik;
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
Če tudi so ga hoteli varati z usti svojimi, in so z jezikom svojim lagali se njemu,
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
In srce njihovo ni bilo obrneno proti njemu, in niso bili stanovitni v zavezi njegovi:
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
Vendar je on usmiljen opíral krivico, tako da jih ni pogubil; in odvračal je svoj srd obilo, in ní vnemal vse jeze svoje,
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
Spomnivši se, da so meso, veter, ki gre in se ne vrne.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Kolikokrat so ga razdražili v puščavi; žalili so ga v samoti!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Ki so hitro izkušali Boga mogočnega, in žalili Svetega Izraelovega.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Ne spomnivši se roke njegove, dné, ko jih je bil otél sovražnika.
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
Ko je v Egiptu delal znamenja svoja, in čuda svoja na polji Taniškem.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
Ko je v kri izpremenil njih potoke, in reke njih, da bi ne mogli piti.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
Izpustil je nad njé živali krdelo, da bi jih pokončalo, in žabe, da jih uničijo.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
In dal je njih sad murnu in kobilici njih delo.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
Pobil je s točo njih trte in smokve njih z ognjem, ki je pokončal vse, kamor je prišel.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
Dal je tudi isti toči njih živali, in njih čede žarjavici ognjeni.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
Izpustil je nad nje jeze svoje žar, srd in nevoljo in stisko, pošiljajoč oznanovalce nesreče.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
Pretehtal je k jezi svoji pot, smrti ni ubranil njih življenja; in živali njih izročil je kugi.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
In udaril je vse prvorojeno v Egiptu; prvino moči v šatorih Kamovih.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
In prepeljal je kakor ovce ljudstvo svoje, in vodil jih je kakor čede po puščavi.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
In peljal jih je varno tako, da se niso bali, potem ko je bilo morje pokrilo njih sovražnike.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
Pripeljal jih je do meje svetosti svoje, gore té, katero je pridobila desnica njegova.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
Izgnal je izpred njih obličja narode in storil, da so pripali vrvi posesti in prebivali so v njih šatorih Izraelovi rodovi.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Vendar so izkušali in razdražili Boga najvišjega, in pričanj njegovih niso se držali.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Temuč obrnili so se ter ravnali izdajalsko, kakor njih pradedje; obrnili so se kakor lok goljufen,
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Ker dražili so ga z višinami svojimi in svojimi maliki, do ljubosumnosti so ga razvneli.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
Slišal je Bog in se razsrdil, in zavrgel je silno Izraela.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
Tako, da je zapustivši prebivališče v Silu, šator, katerega je bil postavil med ljudmi,
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
Dal v sužnjost svojo moč, in slavo svojo sovražniku v pest.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
In izročil je meču ljudstvo svoje, ker se je bil razsrdil zoper posestvo svoje.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Ogenj je pokončal mladeniče njegove, in device njegove niso se hvalile.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Duhovniki njegovi padli so pod mečem, in vdove njegove niso jokale.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Potem se je zbudil Gospod, kakor da bi bil spal, kakor korenjak, pojoč po vinu.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
In udaril je sovražnike svoje nazaj; sramoto večno jim je naložil.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Slednjič je zavrgel šator Jožefov in rodú Efrajmovega ni izvolil.
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
Izvolil pa je rod Judov, goro Sijonsko, da bi jo ljubil.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
Zidal je enako najvišjim gradovom svetišče svoje, namreč v deželi, katero je utrdil.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
In izvolil je Davida hlapca svojega, in vzel ga iz ograje čede,
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
Peljal ga je od doječih, da bi pasel Jakoba, ljudstvo svoje in Izraela, posestvo svoje,
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
Kateri jih je pasel po poštenosti srca svojega, in vodil jih je z najvišjo razumnostjo svojih rok.

< Masalimo 78 >