< Masalimo 78 >
1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Ihubo ka-Asafu Zwanini imfundiso yami, bantu bami; lilalele amazwi omlomo wami.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
Ngizavula umlomo wami ngemifanekiso, ngizakutsho izinto ezifihlekileyo, izinto zekadeni,
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
esakuzwayo lesikwaziyo esakutshelwa ngokhokho bethu.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Kasizukuzifihlela abantwana babo; sizasitshela isizukulwane esizayo ngemisebenzi emangalisayo kaThixo, amandla akhe, lemimangaliso aseyenzile.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
Wamisela uJakhobe imithetho wabeka umlayo ko-Israyeli, walaya okhokho bethu ukuthi bawufundise abantwababo,
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
ukuze aziwe yisizukulwane esilandelayo, kanye labantwana abazazalwa, kuthi labo batshele abantwababo.
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
Yikho-ke bazabeka ithemba labo kuNkulunkulu njalo abasoze bakhohlwa izenzo zakhe kodwa bagcine imilayo yakhe.
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
Kabayikuba njengabokhokho babo ababeyisizukulwana esilobuqholo lesihlamukayo, onhliziyo zabo zazingazinikelanga kuNkulunkulu omoya yabo yayingathembekanga kuye.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Amadoda ako-Efrayimi, loba ayehlomile ngemitshoko, afulathela mhla welanga lempi;
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
kabasigcinanga isivumelwano sikaNkulunkulu, bala ukuphila ngomthetho wakhe.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
Bakhohlwa lokho ayekwenzile, izimanga ayebatshengise zona.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Wenza imimangaliso oyise bekhangele elizweni laseGibhithe, esigodini saseZowani.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Walwahlukanisa ulwandle wabahola bachapha; wenza amanzi ema aqina saka njengomduli.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
Wabahola ngeyezi emini njalo ngokukhanya komlilo ubusuku bonke.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
Wawaqhekeza amadwala enkangala wabapha amanzi amanengi njengolwandle;
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
wantshazisa impophoma emadwaleni amawa wenza amanzi ageleza njengemifula.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Kodwa baqhubeka besona phambi kwakhe, bamhlamukela enkangala yena oPhezukonke.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
Bamlinga uNkulunkulu ngabomo ngokucela ukudla ababekutshisekela.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Bamchothoza uNkulunkulu besithi, “Kambe uNkulunkulu angendlala itafula lokudlela enkangala na?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Wathi lapho etshaya idwala, amanzi antshantshaza, kwageleza amanzi amanengi. Kodwa angasipha njalo lokudla na? Angabalethela inyama abantu bakhe na?”
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
UThixo wathi ebezwa wathukuthela kakhulu; umlilo wakhe wavuthela kuJakhobe, ulaka lwakhe lwaqina ku-Israyeli,
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
ngoba kabamkholwanga uNkulunkulu njalo kabawathembanga amandla okuhlenga kwakhe.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Loba kunjalo walaya umkhathi ngaphezulu wavula iminyango yamazulu;
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
wanisa imana ukuthi badle abantu, wabapha amabele asezulwini.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Abantu badla isinkwa sezingilosi; wabathumela konke ukudla ababengakudla.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Wawukhulula umoya wempumalanga uvela emazulwini, wawukhulula umoya weningizimu ngamandla akhe.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Wanisela inyama kubo njengothuli, izinyoni eziphaphayo zaba njengetshebetshebe ogwini lolwandle.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
Wazenza zehlela phakathi kwezihonqo zabo, indawana yonke emathenteni abo.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
Bazitika baze bakhangela, ngoba wayebaphe ababekade bekukhalela.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
Kodwa bengakakutshiyi lokho kudla ababekukhalela belokhu besakunambitha emilonyeni yabo,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
ulaka lukaNkulunkulu lwavutha kubo; wabulala zona iziqwabalanda zabo, wawahemula amajaha ako-Israyeli.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Phezu kwakho konke lokhu baqhubeka besona; phezu kwezimanga zakhe, kabazange bakholwe.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Ngakho wenza insuku zabo zaphelela ezeni njalo leminyaka yabo yagcwala ukwesaba.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Kwakusithi uNkulunkulu angababulala, bamdinge; baphendukele kuye njalo ngokutshiseka.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
Bakhumbula ukuthi uNkulunkulu wayelidwala labo, ukuthi uNkulunkulu oPhezukonke wayenguMhlengi wabo.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
Kodwa-ke kwakuyikumyenga ngemilomo yabo, beqamba amanga kuye ngendimi zabo;
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
inhliziyo zabo zazingabambelelanga kuye, babengathembekanga esivumelwaneni sakhe.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
Kodwa wayelesihawu; wazithethelela izono zabo kaze ababhubhisa. Isikhathi ngesikhathi waluthoba ulaka lwakhe akaze akuqubula konke ukuthukuthela kwakhe.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
Wakhumbula ukuthi babeyinyama nje intshongolo eyedlulayo nje ingabe isabuya.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Kodwa ukuthi bamhlamukela kanengi njani enkangala, bamdabukisa egwaduleni!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Baphindaphinda ukulinga uNkulunkulu; bamthukuthelisa oNgcwele ka-Israyeli.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Kabawakhumbulanga amandla akhe usuku abakhulula ngalo kumncindezeli,
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
usuku lapho aveza khona izibonakaliso zakhe ezimangalisayo eGibhithe, izimanga zakhe esigodini saseZowani.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
Waguqula imifula yabo yaba ligazi; behluleka ukunatha ezifuleni zabo.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
Wathumela imihlambi yezibawu zabantinya, lamaxoxo ababhuqayo.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
Amabele abo wawathela izintethe, izithelo zabo isikhongwane.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
Wathintitha amavini abo ngesiqhotho lemikhiwa yabo yesikhamore wayitshazisa ngongqwaqwane.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
Inkomo zabo wazithela ngesiqhotho, izifuyo zabo zadliwa yizikhatha zombane.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
Wabathululela ulaka lwakhe oluvuthayo, intukuthelo yakhe, ukucunuka lenzondo ixuku lezingilosi ezibhubhisayo.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
Wayilungisa indlela yolaka lwakhe; kabaphephisanga ekufeni kodwa wabanikela emikhuhlaneni.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
Wawabulala wonke amazibulo aseGibhithe, izithelo zabo zokuqala zokuba ngamadoda emathenteni kaHamu.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
Kodwa wabakhupha abantu bakhe njengomhlambi wezimvu; wabahola njengezimvu bedabula inkangala.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
Wabakhokhela ngonanzelelo, ngakho babengesabi; kodwa ulwandle lwazigubuzela izitha zabo.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
Kanjalo wabaletha emngceleni welizwe lakhe elingcwele, elizweni lamaqaqa ayelithethe ngesandla sakhe sokunene.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
Wazixotsha izizwe phambi kwabo wabahlukanisela ilizwe lazo laba yilifa; wahlalisa izizwana zako-Israyeli emizini yazo.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Kodwa bamlinga uNkulunkulu, bamhlamukela oPhezukonke; kabayigcinanga imilayo yakhe.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Njengabokhokho babo babengathembekanga bengakholwa, ungeke wathemba njengedandili elenziwe kubi.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Bamvusa ulaka ngezindawo zabo eziphezulu; baqubula ubukhwele bakhe ngezithombe zabo.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
Wathi uNkulunkulu ngokukuzwa lokho, wathukuthela kakhulu; wamlahla qobo lokumlahla u-Israyeli.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
Walidela ithabanikeli lakhe eShilo, ithente ayelakhile phakathi kwabantu.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
Umphongolo wakhe wamandla wawusa ekuthunjweni, inkazimulo yakhe ezandleni zesitha.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
Abantu bakhe wabanikela ukudliwa yinkemba; wayethukuthele kakhulu ngelifa lakhe.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Umlilo waziqeda izinsizwa zabo, izintombi zabo zaswela izingoma zomtshado;
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
abaphristi babo babulawa ngenkemba, abafelokazi babo behluleka ukulila.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
INkosi yasivuka njengokade esebuthongweni, njengomuntu ephaphama ekudakweni yiwayini.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
Wazitshaya zahlehla izitha zakhe; waziyangisa okungapheliyo.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Khonapho-ke wawakhalala amathente kaJosefa, akaze asikhetha isizwana sika-Efrayimi;
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
kodwa wakhetha isizwana sikaJuda, iNtaba iZiyoni ayeyithanda.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
Wakha indlu yakhe engcwele njengeziqongo, njengomhlaba awumisela ingunaphakade.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
Wakhetha uDavida inceku yakhe wamthatha ezilugwini zezimvu;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
wamsusa ekweluseni izimvu wamletha ukuba ngumelusi wabantu bakhe uJakhobe, baka-Israyeli ilifa lakhe.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
Njalo uDavida wabelusa ngobuqotho benhliziyo; wabakhokhela ngesandla sobungcitshi.