< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Maskil d'Asaph. Mon peuple, écoute ma Loi, prêtez vos oreilles aux paroles de ma bouche.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
J'ouvrirai ma bouche en similitudes: je manifesterai les choses notables du temps d'autrefois.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Lesquelles nous avons ouïes et connues, et que nos pères nous on racontées.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
Nous ne les cèlerons point à leurs enfants, [et] ils raconteront à la génération à venir les louanges de l'Eternel, et sa force, et ses merveilles qu'il a faites.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
Car il a établi le témoignage en Jacob, et il a mis la Loi en Israël; et il donna charge à nos pères de les faire entendre à leurs enfants.
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
Afin que la génération à venir, les enfants, [dis-je], qui naîtraient, les connut, [et] qu'ils se missent en devoir de les raconter à leurs enfants;
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
Et afin qu'ils missent leur confiance en Dieu, et qu'ils n'oubliassent point les exploits du [Dieu] Fort, et qu'ils gardassent ses commandements.
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
Et qu'ils ne fussent point, comme leurs pères, une génération revêche et rebelle, une génération qui n'a point soumis son cœur, et l'esprit de laquelle n'a point été fidèle au [Dieu] Fort.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
Les enfants d'Ephraïm armés entre les archers, ont tourné le dos le jour de la bataille.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
Ils n'ont point gardé l'alliance de Dieu, et ont refusé de marcher selon sa Loi.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
Et ils ont mis en oubli ses exploits et ses merveilles qu'il leur avait fait voir.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Il a fait des miracles en la présence de leurs pères au pays d'Egypte, au territoire de Tsohan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
Il a fendu la mer, et les a fait passer au travers, et il a fait arrêter les eaux comme un monceau [de pierre].
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
Et il les a conduits de jour par la nuée, et toute la nuit par une lumière de feu.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
Il a fendu les rochers au désert, et leur a donné abondamment à boire, comme [s'il eût puisé] des abîmes.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
Il a fait, dis-je, sortir des ruisseaux de la roche, et en a fait découler des eaux comme des rivières.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Toutefois ils continuèrent à pécher contre lui, irritant le Souverain au désert.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
Et ils tentèrent le [Dieu] Fort dans leurs cœurs, en demandant de la viande qui flattât leur appétit.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Ils parlèrent contre Dieu, disant: le [Dieu] Fort nous pourrait-il dresser une table en ce désert?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Voilà, [dirent-ils], il a frappé le rocher, et les eaux en sont découlées, et il en est sorti des torrents abondamment, mais pourrait-il aussi nous donner du pain? apprêterait-il bien de la viande à son peuple?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
C'est pourquoi l'Eternel les ayant ouïs, se mit en grande colère, et le feu s'embrasa contre Jacob, et sa colère s'excita contre Israël.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Parce qu'ils n'avaient point cru en Dieu, et ne s'étaient point confiés en sa délivrance.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Bien qu'il eût donné commandement aux nuées d'en haut, et qu'il eût ouvert les portes des cieux;
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
Et qu'il eût fait pleuvoir la manne sur eux afin qu'ils en mangeassent, et qu'il leur eût donné le froment des cieux;
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Tellement que chacun mangeait du pain des puissants. Il leur envoya donc de la viande pour s'en rassasier.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Il excita dans les cieux le vent d'Orient, et il amena par sa force le vent du midi.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Et il fit pleuvoir sur eux de la chair comme de la poussière, et des oiseaux volants, en une quantité pareille au sable de la mer.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
Et il la fit tomber au milieu de leur camp, [et] autour de leurs pavillons.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
Et ils en mangèrent, et en furent pleinement rassasiés, car il avait accompli leur souhait.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
[Mais] ils n'en avaient pas encore perdu l'envie, et leur viande était encore dans leur bouche.
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
Quand la colère de Dieu s'excita contre eux, et qu'il mit à mort les gras d'entre eux, et abattit les gens d'élite d'Israël.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
Nonobstant cela, ils péchèrent encore, et n'ajoutèrent point de foi à ses merveilles.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
C'est pourquoi il consuma soudainement leurs jours, et leurs années promptement.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
Quand il les mettait à mort, alors ils le recherchaient, ils se repentaient, et ils cherchaient le [Dieu] Fort dès le matin.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
Et ils se souvenaient que Dieu était leur rocher, et que le [Dieu] Fort et Souverain était celui qui les délivrait.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
Mais ils faisaient beau semblant de leur bouche, et ils lui mentaient de leur langue;
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
Car leur cœur n'était point droit envers lui, et ils ne furent point fidèles en son alliance.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
Toutefois, comme il est pitoyable, il pardonna leur iniquité, tellement qu'il ne les détruisit point, mais il apaisa souvent sa colère, et n'émut point toute sa fureur.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
Et il se souvint qu'ils n'étaient que chair, qu'un vent qui passe, et qui ne revient point.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
Combien de fois l'ont-ils irrité au désert, et combien de fois l'ont-ils ennuyé dans ce lieu inhabitable?
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Car coup sur coup ils tentaient le [Dieu] Fort; et bornaient le Saint d'Israël.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
Ils ne se sont point souvenus de sa main, ni du jour qu'il les avait délivrés de la main de celui qui les affligeait.
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
[Ils ne se sont point souvenus] de celui qui avait fait ses signes en Egypte, et ses miracles au territoire de Tsohan:
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
Et qui avait changé en sang leurs rivières et leurs ruisseaux, afin qu'ils n'en pussent point boire.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
Et qui avait envoyé contre eux une mêlée de bêtes, qui les mangèrent; et des grenouilles, qui les détruisirent.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
Et qui avait donné leurs fruits aux vermisseaux, et leur travail aux sauterelles.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
Qui avait détruit leurs vignes par la grêle, et leurs sycomores par les orages.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
Et qui avait livré leur bétail à la grêle, et leurs troupeaux aux foudres étincelantes.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
Qui avait envoyé sur eux l'ardeur de sa colère, grande colère, indignation et détresse, [qui sont] un envoi de messagers de maux.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
Qui avait dressé le chemin à sa colère, et n'avait point retiré leur âme de la mort; et qui avait livré leur bétail à la mortalité.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
Et qui avait frappé tout premier-né en Egypte, les prémices de la vigueur dans les tentes de Cam.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
Qui avait fait partir son peuple comme des brebis; et qui l'avait mené par le désert comme un troupeau.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
Et qui les avait conduits sûrement, et sans qu ils eussent aucune frayeur, là où la mer couvrit leurs ennemis.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
Et qui les avait introduits en la contrée de sa Sainteté, [savoir] en cette montagne que sa droite a conquise.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
Et qui avait chassé de devant eux les nations qu'il leur a fait tomber en lot d'héritage, et avait fait habiter les Tribus d'Israël dans les tentes de ces nations.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Mais ils ont tenté et irrité le Dieu Souverain, et n'ont point gardé ses témoignages.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Et ils se sont retirés en arrière, et se sont portés infidèlement, ainsi que leurs pères; ils se sont renversés comme un arc qui trompe.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
Et ils l'ont provoqué à la colère par leurs hauts lieux, et l'ont ému à la jalousie par leurs images taillées.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
Dieu l'a ouï, et s'est mis en grande colère, et il a fort méprisé Israël.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
Et il a abandonné le pavillon de Silo, le Tabernacle où il habitait entre les hommes.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
Et il a livré en captivité sa force et son ornement entre les mains de l'ennemi.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
Et il a livré son peuple à l'épée et s'est mis en grande colère contre son héritage.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Le feu a consumé leurs gens d'élite, et leurs vierges n'ont point été louées.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Leurs Sacrificateurs sont tombés par l'épée, et leurs veuves ne les ont point pleuré.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Puis le Seigneur s'est réveillé comme un homme qui se serait endormi, et comme un puissant homme qui s'écrie ayant encore le vin dans la tête.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
Et il a frappé ses adversaires par derrière, et les a mis en opprobre perpétuel.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Mais il a dédaigné le Tabernacle de Joseph, et n'a point choisi la Tribu d'Ephraïm.
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
Mais il a choisi la Tribu de Juda, la montagne de Sion, laquelle il aime;
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
Et il a bâti son Sanctuaire comme [des bâtiments] haut élevés, et l'a établi comme la terre qu'il a fondée pour toujours.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
Et il a choisi David, son serviteur, et l'a pris des parcs des brebis;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
[Il l'a pris, dis-je, ] d'après les brebis qui allaitent, et l'a amené pour paître Jacob son peuple, et Israël son héritage.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
Aussi les a-t-il fait repus selon l'intégrité de son cœur, et conduits par la sage direction de ses mains.

< Masalimo 78 >