< Masalimo 78 >
1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
“A psalm of Asaph.” Give ear, O my people, to my instruction! Incline your ears to the words of my mouth!
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I will open my mouth in a psalm; I will utter sayings of ancient times.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
What we have heard and learned, And our fathers have told us,
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
We will not hide from their children; Showing to the generation to come the praises of Jehovah, His might, and the wonders he hath wrought.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
For he appointed statutes in Jacob, And established a law in Israel, Which he commanded our fathers To make known to their children;
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
So that the generation to come might know them; The children, which should be born, and rise up, Who should declare them to their children;
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
That they might put their trust in God, And not forget his deeds, But keep his commandments;
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
And might not be, like their forefathers, A stubborn and rebellious generation, —A generation whose heart was not fixed upon God, And whose spirit was not steadfast toward the Almighty.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The children of Ephraim were like armed bowmen, Who turn their backs in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They kept not the covenant of God, And refused to walk in his law;
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
And forgot his mighty deeds, And the wonders he had shown them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Marvellous things did he in the sight of their fathers, In the land of Egypt, in the field of Zoan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He divided the sea, and caused them to pass through; Yea, he made the waters to stand as a heap.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
By day he led them by a cloud, And all the night by a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He clave the rocks in the wilderness, And gave them drink, as from the great deep.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
From the rock he brought flowing streams, And made water to run down like rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
Yet still they sinned against him, And provoked the Most High in the desert.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
They tempted God in their hearts, By asking food for their delight.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Yea, they spake against God, and said, “Can God spread a table in the wilderness?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Behold! he smote the rock, and the water flowed, And streams gushed forth: Is he also able to give bread? Can he provide flesh for his people?”
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
When, therefore, the LORD heard this, he was wroth: So a fire was kindled against Jacob, And anger arose against Israel.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Because they believed not in God, And trusted not in his aid.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Yet he had commanded the clouds above, And had opened the doors of heaven;
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
And had rained down upon them manna for food, And had given them the corn of heaven.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Every one ate the food of princes; He sent them bread to the full.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
Then he caused a strong wind to blow in the heavens, And by his power he brought a south wind;
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
He rained down flesh upon them as dust, And feathered fowls as the sand of the sea.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
He caused them to fall in the midst of their camp, Round about their habitations.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
So they did eat, and were filled; For he gave them their own desire.
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
Their desire was not yet satisfied, And their meat was yet in their mouths,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
When the wrath of God came upon them, And slew their strong men, And smote down the chosen men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
For all this they sinned still, And put no trust in his wondrous works.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Therefore he consumed their days in vanity, And their years in sudden destruction.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he slew them, they sought him; They returned, and sought earnestly for God;
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
And remembered that God was their rock, And the Most High their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
But they only flattered him with their mouths, And spake falsely to him with their tongues.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
For their hearts were not true to him, Nor were they steadfast in his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
Yet, being full of compassion, he forgave their iniquity, And would not utterly destroy them; Often he restrained his indignation, And stirred not up all his anger.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
He remembered that they were but flesh, —A breath, that passeth and cometh not back.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
How often did they provoke him in the wilderness! How often did they anger him in the desert!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Again and again they tempted God, And offended the Holy One of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They remembered not his hand, Nor the day when he delivered them from the enemy;
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
What signs he had wrought in Egypt, And what wonders in the fields of Zoan.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
He turned their rivers into blood, So that they could not drink of their streams.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent amongst them flies, which devoured them, And frogs, which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
He gave also their fruits to the caterpillar, And their labor to the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
He destroyed their vines with hail, And their sycamore-trees with frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
He also gave up their cattle to hail, And their flocks to hot thunderbolts.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He sent against them the fierceness of his anger, Wrath, indignation, and woe, —A host of angels of evil.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made a way for his anger, He spared them not from death, But gave up their lives to the pestilence.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
He smote all the firstborn in Egypt; The first-fruits of their strength in the tents of Ham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
But he led forth his own people like sheep, And guided them like a flock in the wilderness.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
He led them on safely, so that they feared not, While the sea overwhelmed their enemies.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
He brought them to his own sacred border, Even to this mountain which his right hand had gained.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
He cast out the nations before them, And divided their land by a measuring-line, as an inheritance, And caused the tribes of Israel to dwell in their tents.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they tempted and provoked God, the Most High, And kept not his statutes;
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
Like their fathers they were faithless, and turned back; They turned aside, like a deceitful bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
They provoked his anger by their high places, And stirred up his jealousy by their graven images.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
God saw this, and was wroth, And greatly abhorred Israel;
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
So that he forsook the habitation at Shiloh, The tabernacle where he dwelt among men,
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
And delivered his strength into captivity, And his glory into the hand of the enemy.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
His own people he gave up to the sword, And was wroth with his own inheritance.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fire consumed their young men, And their maidens did not bewail them.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword, And their widows made no lamentation.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
But at length the Lord awaked as from sleep, As a hero who had been overpowered by wine;
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
He smote his enemies, and drove them back, And covered them with everlasting disgrace.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Yet he rejected the tents of Joseph, And chose not the tribe of Ephraim;
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
But chose the tribe of Judah, The Mount Zion which he loved;
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
Where he built, like the heavens, his sanctuary; Like the earth, which he hath established for ever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
And he chose David, his servant, And took him from the sheepfolds;
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
From tending the suckling ewes he brought him To feed Jacob his people, And Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
He fed them with an upright heart, And guided them with skilful hands.