< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Maschil of Asaph. Give ear, O my people, [to] my law: incline your ears to the words of my mouth.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I will open my mouth in a parable: I will utter dark sayings of old:
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
Which we have heard and known, and our fathers have told us.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
We will not hide [them] from their children, shewing to the generation to come the praises of the LORD, and his strength, and his wonderful works that he hath done.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
For he established a testimony in Jacob, and appointed a law in Israel, which he commanded our fathers, that they should make them known to their children:
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
That the generation to come might know [them, even] the children [which] should be born; [who] should arise and declare [them] to their children:
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
That they might set their hope in God, and not forget the works of God, but keep his commandments:
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
And might not be as their fathers, a stubborn and rebellious generation; a generation [that] set not their heart aright, and whose spirit was not stedfast with God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The children of Ephraim, [being] armed, [and] carrying bows, turned back in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They kept not the covenant of God, and refused to walk in his law;
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
And forgat his works, and his wonders that he had shewed them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Marvellous things did he in the sight of their fathers, in the land of Egypt, [in] the field of Zoan.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He divided the sea, and caused them to pass through; and he made the waters to stand as an heap.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
In the daytime also he led them with a cloud, and all the night with a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He clave the rocks in the wilderness, and gave [them] drink as [out of] the great depths.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
He brought streams also out of the rock, and caused waters to run down like rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
And they sinned yet more against him by provoking the most High in the wilderness.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
And they tempted God in their heart by asking meat for their lust.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
Yea, they spake against God; they said, Can God furnish a table in the wilderness?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Behold, he smote the rock, that the waters gushed out, and the streams overflowed; can he give bread also? can he provide flesh for his people?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Therefore the LORD heard [this], and was wroth: so a fire was kindled against Jacob, and anger also came up against Israel;
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Because they believed not in God, and trusted not in his salvation:
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
Though he had commanded the clouds from above, and opened the doors of heaven,
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
And had rained down manna upon them to eat, and had given them of the corn of heaven.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Man did eat angels’ food: he sent them meat to the full.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He caused an east wind to blow in the heaven: and by his power he brought in the south wind.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
He rained flesh also upon them as dust, and feathered fowls like as the sand of the sea:
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
And he let [it] fall in the midst of their camp, round about their habitations.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
So they did eat, and were well filled: for he gave them their own desire;
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
They were not estranged from their lust. But while their meat [was] yet in their mouths,
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
The wrath of God came upon them, and slew the fattest of them, and smote down the chosen [men] of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
For all this they sinned still, and believed not for his wondrous works.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
Therefore their days did he consume in vanity, and their years in trouble.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he slew them, then they sought him: and they returned and enquired early after God.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
And they remembered that God [was] their rock, and the high God their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
Nevertheless they did flatter him with their mouth, and they lied unto him with their tongues.
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
For their heart was not right with him, neither were they stedfast in his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he, [being] full of compassion, forgave [their] iniquity, and destroyed [them] not: yea, many a time turned he his anger away, and did not stir up all his wrath.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
For he remembered that they [were but] flesh; a wind that passeth away, and cometh not again.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
How oft did they provoke him in the wilderness, [and] grieve him in the desert!
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
Yea, they turned back and tempted God, and limited the Holy One of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They remembered not his hand, [nor] the day when he delivered them from the enemy.
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
How he had wrought his signs in Egypt, and his wonders in the field of Zoan:
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
And had turned their rivers into blood; and their floods, that they could not drink.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent divers sorts of flies among them, which devoured them; and frogs, which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
He gave also their increase unto the caterpiller, and their labour unto the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
He destroyed their vines with hail, and their sycomore trees with frost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
He gave up their cattle also to the hail, and their flocks to hot thunderbolts.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
He cast upon them the fierceness of his anger, wrath, and indignation, and trouble, by sending evil angels [among them].
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made a way to his anger; he spared not their soul from death, but gave their life over to the pestilence;
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
And smote all the firstborn in Egypt; the chief of [their] strength in the tabernacles of Ham:
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
But made his own people to go forth like sheep, and guided them in the wilderness like a flock.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
And he led them on safely, so that they feared not: but the sea overwhelmed their enemies.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
And he brought them to the border of his sanctuary, [even to] this mountain, [which] his right hand had purchased.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
He cast out the heathen also before them, and divided them an inheritance by line, and made the tribes of Israel to dwell in their tents.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they tempted and provoked the most high God, and kept not his testimonies:
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
But turned back, and dealt unfaithfully like their fathers: they were turned aside like a deceitful bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
For they provoked him to anger with their high places, and moved him to jealousy with their graven images.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
When God heard [this], he was wroth, and greatly abhorred Israel:
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
So that he forsook the tabernacle of Shiloh, the tent [which] he placed among men;
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
And delivered his strength into captivity, and his glory into the enemy’s hand.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
He gave his people over also unto the sword; and was wroth with his inheritance.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
The fire consumed their young men; and their maidens were not given to marriage.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword; and their widows made no lamentation.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
Then the Lord awaked as one out of sleep, [and] like a mighty man that shouteth by reason of wine.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
And he smote his enemies in the hinder parts: he put them to a perpetual reproach.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
Moreover he refused the tabernacle of Joseph, and chose not the tribe of Ephraim:
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
But chose the tribe of Judah, the mount Zion which he loved.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
And he built his sanctuary like high [palaces], like the earth which he hath established for ever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
He chose David also his servant, and took him from the sheepfolds:
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
From following the ewes great with young he brought him to feed Jacob his people, and Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
So he fed them according to the integrity of his heart; and guided them by the skilfulness of his hands.

< Masalimo 78 >