< Masalimo 78 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
Understanding for Asaph. Attend, O my people, to my law: incline your ears to the words of my mouth.
2 Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
I will open my mouth in parables: I will utter propositions from the beginning.
3 zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
How great things have we heard and known, and our fathers have told us.
4 Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
They have not been hidden from their children, in another generation. Declaring the praises of the Lord, and his powers, and his wonders which he hath done.
5 Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
And he set up a testimony in Jacob: and made a law in Israel. How great things he commanded our fathers, that they should make the same known to their children:
6 kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
That another generation might know them. The children that should be born and should rise up, and declare them to their children.
7 Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
That they may put their hope in God and may not forget the works of God: and may seek his commandments.
8 Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
That they may not become like their fathers, a perverse and exasperating generation. A generation that set not their heart aright: and whose spirit was not faithful to God.
9 Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
The sons of Ephraim who bend and shoot with the bow: they have turned back in the day of battle.
10 iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
They kept not the covenant of God: and in his law they would not walk.
11 Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
And they forgot his benefits, and his wonders that he had shewn them.
12 Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
Wonderful things did he do in the sight of their fathers, in the land of Egypt, in the field of Tanis.
13 Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
He divided the sea and brought them through: and he made the waters to stand as in a vessel.
14 Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
And he conducted them with a cloud by day: and all the night with a light of fire.
15 Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
He struck the rock in the wilderness: and gave them to drink, as out of the great deep.
16 Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
He brought forth water out of the rock: and made streams run down as rivers.
17 Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
And they added yet more sin against him: they provoked the most High to wrath in the place without water.
18 Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
And they tempted God in their hearts, by asking meat for their desires.
19 Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
And they spoke ill of God: they said: Can God furnish a table in the wilderness?
20 Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
Because he struck the rock, and the waters gushed out, and the streams overflowed. Can he also give bread, or provide a table for his people?
21 Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
Therefore the Lord heard, and was angry: and a fire was kindled against Jacob, and wrath came up against Israel.
22 pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
Because they believed not in God: and trusted not in his salvation.
23 Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
And he had commanded the clouds from above, and had opened the doors of heaven.
24 anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
And had rained down manna upon them to eat, and had given them the bread of heaven.
25 Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
Man ate the bread of angels: he sent them provisions in abundance.
26 Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
He removed the south wind from heaven: and by his power brought in the southwest wind.
27 Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
And he rained upon them flesh as dust: and feathered fowls like as the sand of the sea.
28 Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
And they fell in the midst of their camp, round about their pavilions.
29 Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
So they did eat, and were filled exceedingly, and he gave them their desire:
30 Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
They were not defrauded of that which they craved. As yet their meat was in their mouth:
31 mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
And the wrath of God came upon them. And he slew the fat ones amongst them, and brought down the chosen men of Israel.
32 Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
In all these things they sinned still: and they believed not for his wondrous works.
33 Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
And their days were consumed in vanity, and their years in haste.
34 Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
When he slew them, then they sought him: and they returned, and came to him early in the morning.
35 Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
And they remembered that God was their helper: and the most high God their redeemer.
36 Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
And they loved him with their mouth: and with their tongue they lied unto him:
37 Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
But their heart was not right with him: nor were they counted faithful in his covenant.
38 Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
But he is merciful, and will forgive their sins: and will not destroy them. And many a time did he turn away his anger: and did not kindle all his wrath.
39 Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
And he remembered that they are flesh: a wind that goeth and returneth not.
40 Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
How often did they provoke him in the desert: and move him to wrath in the place without water?
41 Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
And they turned back and tempted God: and grieved the holy one of Israel.
42 Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
They remembered not his hand, in the day that he redeemed them from the hand of him that afflicted them:
43 tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
How he wrought his signs in Egypt, and his wonders in the field of Tanis.
44 Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
And he turned their rivers into blood, and their showers that they might, not drink.
45 Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
He sent amongst them divers sores of flies, which devoured them: and frogs which destroyed them.
46 Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
And he gave up their fruits to the blast, and their labours to the locust.
47 Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
And he destroyed their vineyards with hail, and their mulberry trees with hoarfrost.
48 Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
And he gave up their cattle to the hail, and their stock to the fire.
49 Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
And he sent upon them the wrath of his indignation: indignation and wrath and trouble, which he sent by evil angels.
50 Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
He made a way for a path to his anger: he spared not their souls from death, and their cattle he shut up in death.
51 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
And he killed all the firstborn in the land of Egypt: the firstfruits of all their labour in the tabernacles of Cham.
52 Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
And he took away his own people as sheep: and guided them in the wilderness like a flock.
53 Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
And he brought them out in hope, and they feared not: band the sea overwhelmed their enemies.
54 Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
And he brought them into the mountain of his sanctuary: the mountain which his right hand had purchased. And he cast out the Gentiles before them: and by lot divided to them their land by a line of distribution.
55 Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
And he made the tribes of Israel to dwell in their tabernacles.
56 Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
Yet they tempted, and provoked the most high God: and they kept not his testimonies.
57 Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
And they turned away, and kept not the covenant: even like their fathers they were turned aside as a crooked bow.
58 Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
They provoked him to anger on their hills: and moved him to jealousy with their graven things.
59 Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
God heard, and despised them, and he reduced Israel exceedingly as it were to nothing.
60 Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
And he put away the tabernacle of Silo, his tabernacle where he dwelt among men.
61 Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
And he delivered their strength into captivity: and their beauty into the hands of the enemy.
62 Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
And he shut up his people under the sword: and he despised his inheritance.
63 Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
Fire consumed their young men: and their maidens were not lamented.
64 ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
Their priests fell by the sword: and their widows did not mourn.
65 Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
And the Lord was awaked as one out of sleep, and like a mighty man that hath been surfeited with wine.
66 Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
And he smote his enemies on the hinder parts: he put them to an everlasting reproach.
67 Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
And he rejected the tabernacle of Joseph: and chose not the tribe of Ephraim:
68 Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
But he chose the tribe of Juda, mount Sion which he loved.
69 Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
And he built his sanctuary as of unicorns, in the land which he founded for ever.
70 Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
And he chose his servant David, and took him from the hocks of sheep: he brought him from following the ewes great with young,
71 kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
To feed Jacob his servant, and Israel his inheritance.
72 Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.
And he fed them in the innocence of his heart: and conducted them by the skillfulness of his hands.

< Masalimo 78 >