< Masalimo 77 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
S svojim glasom sem klical k Bogu, celó s svojim glasom k Bogu in mi je prisluhnil.
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
Na dan svoje stiske sem iskal Gospoda. Moja vnetja so se gnojila ponoči in niso odnehala. Moja duša je odklanjala, da bi bila potolažena.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
Spomnil sem se Boga in bil vznemirjen. Pritoževal sem se in moj duh je bil nadvladan. (Sela)
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Moje oči držiš budne. Tako sem vznemirjen, da ne morem govoriti.
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
Preudarjal sem [o] dneh iz davnine, letih starodavnih časov.
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
Spominjam se svoje pesmi ponoči. Posvetujem se s svojim lastnim srcem in moj duh je storil marljivo preiskavo.
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
›Ali bo Gospod za vedno zavračal ali ne bo več naklonjen?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Je njegovo usmiljenje popolnoma odšlo za vedno? Ali njegova obljuba odpove na vékomaj?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Je Bog pozabil biti milostljiv? Ali je v jezi zaprl svoja nežna usmiljenja?‹ (Sela)
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
Rekel sem: »To je moja šibkost, toda spominjal se bom let desnice Najvišjega.«
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
Spominjal se bom Gospodovih del. Zagotovo se bom spominjal tvojih čudežev od davnine.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
Premišljeval bom tudi o vsem tvojem delu in govoril o tvojih dejanjih.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
Tvoja pot, oh Bog, je v svetišču. Kdo je tako velik Bog kakor naš Bog?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Ti si Bog, ki dela čudeže. Med ljudstvom si oznanil svojo moč.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
S svojim laktom si odkupil svoje ljudstvo, Jakobove in Jožefove sinove. (Sela)
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
Vode so te videle, oh Bog, vode so te videle, bile so prestrašene. Tudi globine so bile vznemirjene.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
Oblaki so izlivali vodo, nebo je pošiljalo zvok, tudi tvoje puščice so šle daleč.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
Zvok tvojega groma je bil na nebu, bliski so razsvetljevali zemeljski [krog], zemlja je trepetala in se tresla.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
Tvoja pot je na morju in tvoja steza v velikih vodah in tvoje stopinje niso znane.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Svoje ljudstvo vodiš kakor trop z Mojzesovo in Aronovo roko.