< Masalimo 77 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Wuta na buku ya mokambi ya bayembi, kolanda Yedutuni. Nzembo ya Azafi. Nabelelaka Nzambe na koganga; nabelelaka Nzambe mpo ete ayoka ngai!
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
Tango nazalaka na pasi, nalukaka Nkolo; na butu, nalembaka te kotombola maboko na ngai mpe naboyaka kobondisama.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
Nakanisaka Nzambe mpe nalelaka, nakotaka na mozindo ya makanisi mpe nalembaka nzoto.
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Opimelaka miso na ngai pongi, namitungisaka mpe nayebaka lisusu te eloko ya koloba.
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
Nakanisaka lisusu mikolo ya kala, mibu nyonso oyo eleka;
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
Na butu, nakanisaka lisusu banzembo na ngai; motema na ngai ezongelaka kokanisa, mpe molimo na ngai ekomaka komituna:
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
« Boni, Nkolo akobwaka biso penza mpo na libela? Akosalela biso lisusu bolamu te?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Bolingo na Ye esili penza mpo na libela? Bilaka na Ye ekokokisama te mpo na libela?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Nzambe abosani solo kosala ngolu? Akangi penza motema na Ye mpo na kanda? »
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
Mpe namilobelaka: « Tala likambo oyo ezali kosala ngai pasi: loboko ya mobali ya Ye-Oyo-Aleki-Likolo ebongwani! »
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
Nakanisaka misala minene ya Yawe, bikamwa na Yo ya kala.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
Nakanisaka nyonso oyo osalaki kino na bikamwa na Yo.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
Oh Nzambe, banzela na Yo ezali bule; nzambe nini akokani na Yo na monene?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Ozali Nzambe oyo asalaka bikamwa; olakisi nguya na Yo kati na bikolo.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
Na nguya ya loboko na Yo, okangolaki bato na Yo, bakitani ya Jakobi mpe ya Jozefi.
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
Oh Nzambe, mayi emonaki Yo! Mayi emonaki Yo mpe ekomaki kolenga; ezala mozindo ya mayi eninganaki.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
Mapata esopaki mayi ebele, likolo eyokisaki lokito ya kake, mpe makonga na Yo ezalaki koleka-leka na bangambo nyonso.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
Na lokito ya kake na Yo, mikalikali engengisaki mokili, mabele eninganaki mpe elengaki.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
Opasolaki nzela kati na ebale monene, balabala na Yo kati na mayi monene, mpe moto moko te amonaki bilembo ya matambe na Yo.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Otambolisaki bato na Yo lokola etonga, na loboko ya Moyize mpe ya Aron.