< Masalimo 77 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Asaphin Psalmi, Jedutunin edestä, edelläveisaajalle. Minä huudan äänelläni Jumalaa: Jumalaa minä huudan, ja hän kuultelee minua.
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
Minun hätä-ajallani etsin minä Herraa: minun käteni on yöllä ojettu, ja ei lakkaa; sillä ei minun sieluni salli itseänsä lohduttaa.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
Minä ajattelen tosin Jumalan päälle, olen kuitenkin murheissani: minä tutkin, ja henkeni on sittekin ahdistuksessa, (Sela)
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Sinä pidät minun silmäni, että he valvovat: minä olen niin voimatoin, etten minä voi puhua.
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
Minä ajattelen vanhoja aikoja, entisiä vuosia:
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
Minä muistan yöllä minun kantelettani: minä puhun sydämelleni, ja minun henkeni tutkii:
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Heittäneekö Jumala pois ijankaikkisesti, ja ei yhtään armoa silleen osoittane?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Puuttuneeko hänen laupiutensa ijankaikkisesti, ja olleeko lupauksella jo loppu suvusta sukuhun?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Onko Jumala unohtanut olla armollinen? ja sulkenut laupiutensa vihan tähden? (Sela)
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
Minä sanoin: se on minun heikkouteni; mutta Ylimmäisen oikia käsi voi kaikki muuttaa.
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
Sentähden minä muistan Herran töitä, ja minä ajattelen entisiä ihmeitäs,
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
Ja puhun kaikista sinun töistäs, ja sanon sinun teoistas.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
Jumala, sinun ties on pyhä: kussa on niin väkevää Jumalaa kuin sinä Jumala?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Sinä olet se Jumala, joka ihmeitä tekee: sinä osoitit voimas kansain seassa.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
Sinä lunastit sinun kansas käsivarrellas, Jakobin ja Josephin lapset, (Sela)
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
Vedet näkivät sinun, Jumala, vedet näkivät sinun ja vapisivat, ja syvyydet pauhasivat,
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
Paksut pilvet kaasivat vettä, pilvet jylisivät ja nuolet lensivät sekaan.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
Se jylisi taivaassa, ja sinun leimaukses välkkyi maan piirin päälle: maa liikkui ja värisi siitä.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
Sinun ties oli meressä, ja sinun polkus olivat suurissa vesissä, ja ei sinun jälkiäs kenkään tuntenut.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Sinä veit kansas niinkuin lammaslauman, Moseksen ja Aaronin kautta.

< Masalimo 77 >