< Masalimo 77 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
To the Overseer, for Jeduthun. — A Psalm of Asaph. My voice [is] to God, and I cry, my voice [is] to God, And He hath given ear unto me.
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
In a day of my distress the Lord I sought, My hand by night hath been spread out, And it doth not cease, My soul hath refused to be comforted.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
I remember God, and make a noise, I meditate, and feeble is my spirit. (Selah)
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Thou hast taken hold of the watches of mine eyes, I have been moved, and I speak not.
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
I have reckoned the days of old, The years of the ages.
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
I remember my music in the night, With my heart I meditate, and my spirit doth search diligently:
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
To the ages doth the Lord cast off? Doth He add to be pleased no more?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Hath His kindness ceased for ever? The saying failed to all generations?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Hath God forgotten [His] favours? Hath He shut up in anger His mercies? (Selah)
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
And I say: 'My weakness is, The changes of the right hand of the Most High.'
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
I mention the doings of Jah, For I remember of old Thy wonders,
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
And I have meditated on all Thy working, And I talk concerning Thy doings.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
O God, in holiness [is] Thy way, Who [is] a great god like God?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Thou [art] the God doing wonders. Thou hast made known among the peoples Thy strength,
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
Thou hast redeemed with strength Thy people, The sons of Jacob and Joseph. (Selah)
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
The waters have seen Thee, O God, The waters have seen Thee, They are afraid — also depths are troubled.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
Poured out waters have thick clouds, The skies have given forth a noise, Also — Thine arrows go up and down.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
The voice of Thy thunder [is] in the spheres, Lightnings have lightened the world, The earth hath trembled, yea, it shaketh.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
In the sea [is] Thy way, And Thy paths [are] in many waters, And Thy tracks have not been known.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Thou hast led as a flock Thy people, By the hand of Moses and Aaron!

< Masalimo 77 >