< Masalimo 77 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
“For the leader of the music of the Jeduthunites. A psalm of Asaph.” I call upon God; I cry aloud for help; I call upon God, that he would hear me!
2 Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
In the day of my trouble I seek the Lord; In the night is my hand stretched forth continually; My soul refuseth to be comforted.
3 Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
I remember God, and am disquieted; I think of him, and my spirit is overwhelmed.
4 Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Thou keepest mine eyelids from closing; I am distressed, so that I cannot speak!
5 Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
I think of the days of old, —The years of ancient times.
6 Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
I call to remembrance my songs in the night; I meditate in my heart, And my spirit inquireth:
7 “Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Will the Lord be angry for ever? Will he be favorable no more?
8 Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Is his mercy utterly withdrawn for ever? Doth his promise fail from generation to generation?
9 Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
Hath God forgotten to be gracious? Hath he in anger shut up his compassion?
10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
Then I say, “This is mine affliction, A change in the right hand of the Most High.”
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
I remember the deeds of Jehovah; I think of thy wonders of old.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
I meditate on all thy works, And talk of thy doings.
13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
Thy ways, O God! are holy! Who so great a god as our God?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
Thou art a God who doest wonders; Thou hast manifested thy power among the nations.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
With thy strong arm thou didst redeem thy people, —The sons of Jacob and Joseph.
16 Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
The waters saw thee, O God! The waters saw thee, and feared, And the deep trembled.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
The clouds poured out water, The skies sent forth thunder, And thine arrows flew.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
Thy thunder roared in the whirlwind; Thy lightning illumined the world; The earth trembled and shook.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
Thy way was through the sea, And thy path through great waters; And thy footsteps could not be found.
20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.
Thou didst lead thy people like a flock, By the hands of Moses and Aaron.

< Masalimo 77 >