< Masalimo 76 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
Керівнику хору. На струнних інструментах. Псалом Асафа. Пісня. Відомий в Юдеї Бог, в Ізраїлі величне ім’я Його.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Був у Салемі намет Його, і помешкання Його – на Сіоні.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Там зламав Він полум’яні стріли лука, щит і меч, і війну [припинив]. (Села)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Ти осяяний величчю більше, ніж [ті] гори, [що] здобичі [повні].
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
Міцні серцем стали здобиччю, заснули сном своїм [останнім]; Сильні мужі не можуть поворухнути своїми руками.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Від грізних докорів Твоїх, Боже Якова, застигли колісниця і кінь.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Ти – грізний, хто встоїть перед обличчям Твоїм у час гніву Твого?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
З небес Ти проголосив суд – земля злякалась і затихла,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
коли повстав Бог, щоб судити, щоб врятувати всіх пригнічених землі. (Села)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
Адже навіть гнів людський [обернеться] на славу Тобі, а рештою гніву Ти [переможно] оперезаєш Себе.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Давайте обітниці Господеві, Богові вашому, і виконуйте їх; усі, хто навколо Нього, нехай принесуть дар Грізному.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
Він приборкує дух вождів, страшний Він для царів землі.

< Masalimo 76 >