< Masalimo 76 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
V Judu je Bog poznan. Njegovo ime v Izraelu je veliko.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Tudi v Salemu je njegovo šotorsko svetišče in njegovo bivališče na Sionu.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Tam je prelomil puščice loka, ščit, meč in bitko. (Sela)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Ti si veličastnejši in odličnejši kakor gore plena.
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
Arogantni so oplenjeni, spali so svoje spanje. Nihče izmed mogočnih mož ni našel svojih rok.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Ob tvojem oštevanju, Bog Jakobov, sta tako bojni voz, kakor konj vržena v smrtno spanje.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Ti, celó tebe se je bati in kdo lahko stoji v tvojem pogledu, kadar si jezen?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
Povzročil si, da se z neba sliši sodba; zemlja se je zbala in postala tiha,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
ko je k sodbi vstal Bog, da reši vse krotke na zemlji. (Sela)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
Zagotovo te bo hvalil človeški bes. Ostanek besa boš ti obrzdal.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Zaobljubi se in plačaj Gospodu, svojemu Bogu. Naj vsi tisti, ki so okoli njega, prinesejo darila tistemu, ki bi se ga morali bati.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
Odrezal bo duha princev. Strašen je do zemeljskih kraljev.