< Masalimo 76 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
Psalmus Asaph, in finem, in Laudibus, canticum ad Assyrios. Notus in Iudaea Deus: in Israel magnum nomen eius.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Et factus est in pace locus eius: et habitatio eius in Sion.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Ibi confregit potentias arcum, scutum, gladium, et bellum.
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Illuminans tu mirabiliter a montibus aeternis:
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
turbati sunt omnes insipientes corde. Dormierunt somnum suum: et nihil invenerunt omnes viri divitiarum in manibus suis.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Ab increpatione tua Deus Iacob dormitaverunt qui ascenderunt equos.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Tu terribilis es, et quis resistet tibi? ex tunc ira tua.
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
De caelo auditum fecisti iudicium: terra tremuit et quievit,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
Cum exurgeret in iudicium Deus, ut salvos faceret omnes mansuetos terrae.
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
Quoniam cogitatio hominis confitebitur tibi: et reliquiae cogitationis diem festum agent tibi.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Vovete, et reddite Domino Deo vestro: omnes qui in circuitu eius affertis munera. Terribili
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
et ei qui aufert spiritum principum, terribili apud reges terrae.

< Masalimo 76 >