< Masalimo 76 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
U A ikeia ke Akua ma ka Iuda: Ua kaulana hoi kona inoa ma ka Iseraela.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Aia ma Salema kona halelewa, A ma Ziona hoi kona wahi e noho ai.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Malaila ia i hakihaki ai i na pua o ke kakaka, O ka palekaua hoi, a me ka pahikaua, a me ke koi kaua. (Sila)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Ua oi aku ka hanohano o kou nani mamua o na mauna uliuli.
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
Ua haoia ka poe ikaika o ka naau, A ua moe nui no hoi lakou; Aole i hiki ka lima o ka poe ikaika ke lawelawe.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
No kau papa ana, e ke Akua o Iakoba, Moe iho no ka ke kaakaua a me ka lio.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
O oe, o oe no, ka mea e makauia'i: Owai hoi ka mea e ku ma kou alo, i kou wa e huhu mai ai?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
I loheia no ia oe ka hooponopono ana mai ka lani mai; Makau ae la ka honua, a noho malie iho la,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
I ke ku ana o ke Akua iluna, e hooponopono, E hoola mai hoi i ka poe akahai a pau o ka honua. (Sila)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
E hoonani aku no ka huhu o kanaka ia oe; A e liki no hoi oe i ke koena o ka huhu.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
E hoohiki, a e haawi io aku oukou ia Iehova, i ko oukou Akua: A lawe mai hoi na mea a pau i makana na ka mea e makauia'i.
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
Nana no e hooki ae i ka ikaika o na'lii: He mea weliweli hoi ia no na'lii o ka honua.