< Masalimo 76 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
[Dem Vorsänger, mit Saitenspiel. Ein Psalm von Asaph, ein Lied.] Bekannt ist Gott in Juda, in Israel groß sein Name.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Und in Salem ist [Eig. ward] seine Hütte, und seine Wohnung in Zion.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Dort zerbrach er des Bogens Blitze, Schild und Schwert und Krieg. (Sela)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
Glanzvoller bist du, herrlicher als die Berge des Raubes. [O. Glanzvoll bist du, herrlich von den Bergen des Raubes her]
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
Zur Beute sind geworden die Starkherzigen, sie schlafen ihren Schlaf; und keiner der tapferen Männer fand seine Hände.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
Vor deinem Schelten, Gott Jakobs, sind in tiefen Schlaf gesunken sowohl Wagen als Roß.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Du, du bist furchtbar, und wer kann vor dir bestehen, sobald du erzürnst!
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
Du ließest Gericht hören [d. h. kündigtest Gericht an] von den Himmeln her; die Erde fürchtete sich und ward stille.
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
Als Gott aufstand zum Gericht, um zu retten alle Sanftmütigen des Landes. [O. der Erde] (Sela)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
Denn der Grimm des Menschen wird dich preisen; mit dem Rest des Grimmes wirst du dich gürten.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Tut und bezahlet Gelübde Jehova, eurem Gott; mögen alle, die rings um ihn her sind, Geschenke bringen dem Furchtbaren!
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
Er wird abmähen den Geist [O. das Schnauben] der Fürsten, er ist furchtbar den Königen der Erde.

< Masalimo 76 >