< Masalimo 76 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
Au maître-chantre. — Avec instruments à cordes. — Psaume d'Asaph — Cantique. Dieu s'est fait connaître en Juda; Son nom est grand en Israël.
2 Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
Son tabernacle est à Salem, Et sa résidence à Sion.
3 Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
Là il a brisé les flèches rapides comme l'éclair. Le bouclier, le glaive et les armes de guerre. (Pause)
4 Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
O Tout-Puissant, tu surpasses en majesté Les conquérants les plus glorieux!
5 Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
Ils ont été dépouillés, les hommes au coeur fort; Et tous ces hommes vaillants n'ont plus retrouvé La vigueur de leurs bras.
6 Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
A ta seule menace, ô Dieu de Jacob, Conducteurs de chars et coursiers ont été frappés de torpeur.
7 Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
Mais toi, tu es redoutable! Qui peut tenir devant toi, dès que ta colère éclate?
8 Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
Du haut des cieux, tu fais entendre; La terre est effrayée, et elle se tait,
9 pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
Quand tu te lèves, ô Dieu, pour juger. Pour délivrer tous les opprimés de la terre. (Pause)
10 Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
La fureur même de l'homme tourne à ta louange, Et ton propre courroux est le glaive dont tu restes armé.
11 Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
Faites des voeux, acquittez-les envers l'Éternel, votre Dieu; Que tous les peuples d'alentour viennent offrir Des présents à ce Dieu Redoutable!
12 Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.
Dieu abat l'orgueil des princes; Il est redouté par les rois de la terre.

< Masalimo 76 >