< Masalimo 75 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
برای سالار مغنیان بر لاتهلک. مزمور و سرود آساف تو را حمد می‌گوییم! ای خدا تو راحمد می‌گوییم! زیرا نام تو نزدیک است و مردم کارهای عجیب تو را ذکر می‌کنند.۱
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
هنگامی که به زمان معین برسم براستی داوری خواهم کرد.۲
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
زمین و جمیع ساکنانش گداخته شده‌اند. من ارکان آن را برقرار نموده‌ام، سلاه.۳
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
متکبران را گفتم: «فخر مکنید!» و به شریران که «شاخ خود را میفرازید.۴
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
شاخهای خود را به بلندی میفرازید. و با گردن کشی سخنان تکبرآمیز مگویید.»۵
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
زیرا نه از مشرق و نه از مغرب، و نه ازجنوب سرافرازی می‌آید.۶
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
لیکن خدا، داور است. این را به زیر می‌اندازدو آن را سرافراز می‌نماید.۷
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
زیرا در دست خداوند کاسه‌ای است و باده آن پرجوش. ازشراب ممزوج پر است که از آن می‌ریزد. و امادردهایش را جمیع شریران جهان افشرده، خواهند نوشید.۸
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
و اما من، تا به ابد ذکر خواهم کرد و برای خدای یعقوب ترنم خواهم نمود.۹
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
جمیع شاخهای شریران را خواهم برید و اماشاخهای صالحین برافراشته خواهد شد.۱۰

< Masalimo 75 >