< Masalimo 75 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
Salmo di cantico di Asaf, [dato] al Capo de' Musici, [sopra] Al-tashet NOI ti celebriamo, noi ti celebriamo, o Dio; Perciocchè il tuo Nome [è] vicino; L'uomo racconta le tue maraviglie.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
Al tempo che avrò fissato, Io giudicherò dirittamente.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
Il paese e tutti i suoi abitanti si struggevano; [Ma] io ho rizzate le sue colonne. (Sela)
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Io ho detto agl'insensati: Non siate insensati; Ed agli empi: Non alzate il corno;
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
Non levate il vostro corno ad alto; [E non] parlate col collo indurato.
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
Perciocchè nè di Levante, nè di Ponente, Nè dal deserto, [viene] l'esaltamento.
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
Ma Iddio [è] quel che giudica; Egli abbassa l'uno, ed innalza l'altro.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
Perciocchè il Signore ha in mano una coppa, Il cui vino [è] torbido; Ella [è] piena di mistione, ed egli ne mesce; Certamente tutti gli empi della terra ne succeranno [e] berranno le fecce.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
Ora, quant'è a me, io predicherò [queste cose] in perpetuo, Io salmeggerò all'Iddio di Giacobbe.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
E mozzerò tutte le corna degli empi; E [farò che] le corna de' giusti saranno alzate.