< Masalimo 75 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
Au chef des chantres. Al tachhêt. Psaume d’Assaph. Cantique. Nous te rendons grâce, ô Dieu, nous te rendons grâce, ton nom est près de nous; qu’on proclame tes merveilles!
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
"Quand, dit Dieu, j’en aurai fixé l’heure, je rendrai mes arrêts avec équité.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
Que la terre en soit alarmée avec ses habitants, moi, je raffermirai ses colonnes." (Sélah)
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Je dis aux insensés: "Trêve de folies!" Aux méchants: "Ne relevez point la tête!"
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
Ne relevez pas si haut la tête, ne vous rengorgez pas pour parler avec insolence;
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
car ni de l’orient, ni du couchant, ni du désert ne vient la grandeur.
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
C’Est Dieu qui est l’arbitre: il abaisse l’un, il élève l’autre.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
Car l’Eternel tient une coupe en sa main, où écume un vin tout mêlé d’aromates; de ce vin il verse des rasades, mais la lie, ce sont tous les méchants de la terre qui l’aspirent et la boivent.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
Pour moi, je le proclamerai sans trêve, je chanterai le Dieu de Jacob.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
J’Abattrai toutes les cornes des méchants; les cornes des justes se dresseront bien haut.

< Masalimo 75 >