< Masalimo 75 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
To the chief Musician. 'Destroy not.' A Psalm of Asaph: a Song. Unto thee we give thanks, O God, we give thanks; and thy name is near: thy marvellous works declare it.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
When I shall receive the assembly, I will judge with equity.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
The earth and all the inhabitants thereof are dissolved: I have established its pillars. (Selah)
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
I said unto the boastful, Boast not; and to the wicked, Lift not up the horn:
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
Lift not up your horn on high; speak not arrogantly with a [stiff] neck.
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
For not from the east nor from the west, nor yet from the south doth exaltation [come]:
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
For God is the judge; he putteth down one and exalteth another.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
For in the hand of Jehovah there is a cup, and it foameth with wine, it is full of mixture; and he poureth out of the same; yea, the dregs thereof shall all the wicked of the earth drain off, [and] drink.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
But as for me, I will declare for ever; I will sing psalms to the God of Jacob.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
And all the horns of the wicked will I cut off; [but] the horns of the righteous shall be exalted.

< Masalimo 75 >