< Masalimo 74 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Пентру че, Думнезеуле, не лепезь пентру тотдяуна? Пентру че Те мыний пе турма пэшуний Тале?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Аду-Ць аминте де попорул Тэу пе каре л-ай кыштигат одиниоарэ, пе каре л-ай рэскумпэрат ка семинцие а моштенирий Тале! Аду-Ць аминте де мунтеле Сионулуй, унде Ыць авяй локуинца;
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
ындряптэ-Ць паший спре ачесте локурь пустиите фэрэ курмаре! Врэжмашул а пустиит тотул ын Локашул Тэу чел Сфынт.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Потривничий Тэй ау муӂит ын мижлокул Темплулуй Тэу; шь-ау пус семнеле лор дрепт семне.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
Паркэ ерау ниште оамень каре ридикэ топорул ынтр-о пэдуре дясэ:
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
ын курынд, ау сфэрымат тоате подоабеле сэпате, ку ловитурь де секурь ши чокане.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ау пус фок Сфынтулуй Тэу Локаш; ау дэрымат ши ау пынгэрит локуинца Нумелуй Тэу.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ей зичяу ын инима лор: „Сэ-й прэпэдим пе тоць!” Ау арс тоате локуриле сфинте дин царэ.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
Семнеле ноастре ну ле май ведем; ну май есте ничун пророк ши ну май есте нимень принтре ной каре сэ штие пынэ кынд…
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
Пынэ кынд, Думнезеуле, ва батжокори асуприторул ши ва несокоти врэжмашул фэрэ курмаре Нумеле Тэу?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Пентру че Ыць траӂь ынапой мына ши дряпта Та? Скоате-о дин сын ши нимичеште-й!
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
Тотушь Думнезеу есте Ымпэратул меу, каре дин времурь стрэвекь дэ избэвирь ын мижлокул ачестей цэрь.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Ту ай деспэрцит маря ку путеря Та, ай сфэрымат капетеле балаурилор дин апе;
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
ай здробит капул левиатанулуй, л-ай дат сэ-л мэнынче фяреле дин пустиу.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Ай фэкут сэ цышняскэ извоаре ын пырае, ай ускат рыурь каре ну сякэ.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
А Та есте зиуа, а Та есте ши ноаптя; Ту ай ашезат лумина ши соареле.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Ту ай статорничит тоате хотареле пэмынтулуй, Ту ай рындуит вара ши ярна.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Аду-Ць аминте, Доамне, кэ врэжмашул Те батжокореште ши ун попор некибзуит хулеште Нумеле Тэу!
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Ну лэса прадэ фярелор суфлетул туртурелей Тале ши ну уйта пе вечие вяца ненорочицилор Тэй!
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Ай ын ведере легэмынтул! Кэч локуриле досниче дин царэ сунт плине де бырлогурь де тылхарь.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
Сэ ну се ынтоаркэ рушинат чел апэсат, чи ненорочитул ши сэракул сэ лауде Нумеле Тэу!
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Скоалэ-Те, Думнезеуле, апэрэ-Ць причина! Аду-Ць аминте де окэриле пе каре Ци ле арункэ ын фиекаре зи чел фэрэ минте!
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Ну уйта стригэтеле потривничилор Тэй, зарва каре креште некурмат а челор че се ридикэ ымпотрива Та!

< Masalimo 74 >