< Masalimo 74 >
1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Intelligence d’Asaph.
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Souvenez-vous de votre assemblée, que vous avez possédée dès le commencement. Vous avez racheté la verge de votre héritage: Sion est le mont sur lequel vous avez habité.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Levez vos mains à jamais contre leur orgueil: combien de méchancetés a commises l’ennemi dans votre sanctuaire!
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Ceux qui vous haïssent ont signalé leur orgueil au milieu de votre solennité. Ils ont posé leurs étendards en grand nombre;
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
(Et ils n’ont pas compris ce qu’ils faisaient ), au haut du temple, comme à la sortie d’une ville.
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
Ils ont abattu de concert ses portes: avec la cognée et la hache à double tranchant, ils l’ont renversée.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ils ont brûlé par le feu votre sanctuaire: ils ont souillé sur la terre le tabernacle de votre nom.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ils ont dit dans leur cœur, eux et tous leurs alliés ensemble: Faisons cesser de dessus la terre tous les jours de fêtes de Dieu.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
Nous ne voyons plus nos signes: il n’y a point de prophètes, et Dieu ne nous connaîtra plus.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
Jusques à quand, ô Dieu, l’ennemi se livrera-t-il à l’outrage? notre adversaire irritera-t-il toujours votre nom?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Pourquoi détournez-vous votre main, et votre droite de votre sein pour toujours?
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
Mais Dieu, notre roi depuis des siècles, a opéré le salut au milieu de la terre.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
C’est vous qui, par votre puissance, avez affermi la mer, brisé les têtes des dragons dans les eaux.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
C’est vous qui avez écrasé la tête du dragon: vous l’avez donné pour nourriture aux peuples de l’Éthiopie.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
C’est vous qui avez fait jaillir de la pierre des sources et des torrents; vous avez desséché les fleuves d’Ethan.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
À vous est le jour, et à vous est la nuit: c’est vous qui avez formé l’aurore et le soleil,
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
C’est vous qui avez fait toutes les limites de la terre: l’été et le printemps, c’est vous qui les avez créés.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Souvenez-vous de ceci: l’ennemi a outragé le Seigneur, et un peuple insensé a provoqué votre nom.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Ne livrez pas aux bêtes féroces des âmes qui vous louent; et les âmes de vos pauvres, ne les oubliez pas à jamais.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Jetez les yeux sur votre alliance; parce que ceux qui sont avilis sur la terre ont été comblés de maisons d’iniquités.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
Que celui qui est dans l’humiliation ne soit pas renvoyé couvert de confusion; le pauvre et l’homme sans ressource loueront votre nom.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Levez-vous, ô Dieu, jugez votre cause: souvenez-vous des outrages que vous recevez, de ceux qui vous sont faits par un insensé tout le jour.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
N’oubliez pas les clameurs de vos ennemis: l’orgueil de ceux qui vous haïssent monte toujours.