< Masalimo 74 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
Pour instruire. D’Asaph. Pourquoi, ô Dieu, [nous] as-tu rejetés pour toujours, [et] ta colère fume-t-elle contre le troupeau de ta pâture?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Souviens-toi de ton assemblée, que tu as acquise autrefois, que tu as rachetée pour être la portion de ton héritage, – de la montagne de Sion, où tu as habité.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Élève tes pas vers les ruines perpétuelles; l’ennemi a tout saccagé dans le lieu saint.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Tes adversaires rugissent au milieu des lieux assignés pour ton service; ils ont mis leurs signes pour signes.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
Un homme se faisait connaître quand il élevait la hache dans l’épaisseur de la forêt;
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
Et maintenant, avec des cognées et des marteaux, ils brisent ses sculptures toutes ensemble.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
Ils ont mis le feu à ton sanctuaire, ils ont profané par terre la demeure de ton nom;
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
Ils ont dit en leur cœur: Détruisons-les tous ensemble. Ils ont brûlé tous les lieux assignés [pour le service] de Dieu dans le pays.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
Nous ne voyons plus nos signes; il n’y a plus de prophète, et il n’y a personne avec nous qui sache jusques à quand.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
Jusques à quand, ô Dieu! l’adversaire dira-t-il des outrages? L’ennemi méprisera-t-il ton nom à jamais?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Pourquoi détournes-tu ta main, et ta droite? [Tire-la] de ton sein: détruis!
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
Et Dieu est d’ancienneté mon roi, opérant des délivrances au milieu de la terre.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Tu as fendu la mer par ta puissance, tu as brisé les têtes des monstres sur les eaux;
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
Tu as écrasé les têtes du léviathan, tu l’as donné pour pâture au peuple, – aux bêtes du désert.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Tu as fait sortir la source et le torrent; tu as séché les grosses rivières.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
À toi est le jour, à toi aussi la nuit; toi tu as établi la lune et le soleil.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Tu as posé toutes les bornes de la terre; l’été et l’hiver, c’est toi qui les as formés.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Souviens-toi de ceci, que l’ennemi a outragé l’Éternel! et qu’un peuple insensé a méprisé ton nom.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Ne livre pas à la bête sauvage l’âme de ta tourterelle; n’oublie pas à jamais la troupe de tes affligés.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Regarde à l’alliance! Car les lieux ténébreux de la terre sont pleins d’habitations de violence.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
Que l’opprimé ne s’en retourne pas confus; que l’affligé et le pauvre louent ton nom.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Lève-toi, ô Dieu! plaide ta cause, souviens-toi des outrages que te fait tous les jours l’insensé.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
N’oublie pas la voix de tes adversaires: le tumulte de ceux qui s’élèvent contre toi monte continuellement.

< Masalimo 74 >