< Masalimo 74 >
1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
An Instruction of Asaph. Why, O God, hast Thou cast off for ever? Thine anger smoketh against the flock of Thy pasture.
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Remember Thy company. Thou didst purchase of old, Thou didst redeem the rod of Thy inheritance, This mount Zion — Thou didst dwell in it.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Lift up Thy steps to the perpetual desolations, Everything the enemy did wickedly in the sanctuary.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Roared have thine adversaries, In the midst of Thy meeting-places, They have set their ensigns as ensigns.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
He is known as one bringing in on high Against a thicket of wood — axes.
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
And now, its carvings together With axe and hatchet they break down,
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
They have sent into fire Thy sanctuary, to the earth they polluted the tabernacle of Thy name,
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
They said in their hearts, 'Let us oppress them together,' They did burn all the meeting-places of God in the land.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
Our ensigns we have not seen, There is no more a prophet, Nor with us is one knowing how long.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
Till when, O God, doth an adversary reproach? Doth an enemy despise thy name for ever?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Why dost Thou turn back Thy hand, Even Thy right hand? From the midst of Thy bosom remove [it].
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
And God [is] my king of old, Working salvation in the midst of the earth.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Thou hast broken by Thy strength a sea -[monster], Thou hast shivered Heads of dragons by the waters,
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
Thou hast broken the heads of leviathan, Thou makest him food, For the people of the dry places.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Thou hast cleaved a fountain and a stream, Thou hast dried up perennial flowings.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
Thine [is] the day, also Thine [is] the night, Thou hast prepared a light giver — the sun.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Thou hast set up all the borders of earth, Summer and winter Thou hast formed them.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Remember this — an enemy reproached Jehovah, And a foolish people have despised Thy name.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Give not up to a company, The soul of Thy turtle-dove, The company of Thy poor ones forget not for ever.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Look attentively to the covenant, For the dark places of earth, Have been full of habitations of violence.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
Let not the oppressed turn back ashamed, Let the poor and needy praise Thy name,
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Arise, O God, plead Thy plea, Remember Thy reproach from a fool all the day.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Forget not the voice of Thine adversaries, The noise of Thy withstanders is going up continually!