< Masalimo 74 >
1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
An instruction: of Asaph. Why, O God, hast thou cast off for ever? [why] doth thine anger smoke against the sheep of thy pasture?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Remember thine assembly, which thou hast purchased of old, which thou hast redeemed [to be] the portion of thine inheritance, this mount Zion, wherein thou hast dwelt.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Lift up thy steps unto the perpetual desolations: everything in the sanctuary hath the enemy destroyed.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
Thine adversaries roar in the midst of thy place of assembly; they set up their signs [for] signs.
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
[A man] was known as he could lift up axes in the thicket of trees;
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
And now they break down its carved work altogether, with hatchets and hammers.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
They have set on fire thy sanctuary, they have profaned the habitation of thy name to the ground.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
They said in their heart, Let us destroy them together: they have burned up all God's places of assembly in the land.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
We see not our signs; there is no more any prophet, neither is there among us any that knoweth how long.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
How long, O God, shall the adversary reproach? Shall the enemy contemn thy name for ever?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Why withdrawest thou thy hand, and thy right hand? [pluck it] out of thy bosom: consume [them].
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
But God is my king of old, accomplishing deliverances in the midst of the earth.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Thou didst divide the sea by thy strength; thou didst break the heads of the monsters on the waters:
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
Thou didst break in pieces the heads of leviathan, thou gavest him to be meat to those that people the desert.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Thou didst cleave fountain and torrent, thou driedst up ever-flowing rivers.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
The day is thine, the night also is thine; thou hast prepared the moon and the sun:
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Thou hast set all the borders of the earth; summer and winter — thou didst form them.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Remember this, that an enemy hath reproached Jehovah, and a foolish people have contemned thy name.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Give not up the soul of thy turtle-dove unto the wild beast; forget not the troop of thine afflicted for ever.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Have respect unto the covenant; for the dark places of the earth are full of the dwellings of violence.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
Oh let not the oppressed one return ashamed; let the afflicted and needy praise thy name.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Rise up, O God, plead thine own cause: remember how the foolish man reproacheth thee all the day;
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Forget not the voice of thine adversaries: the tumult of those that rise up against thee ascendeth continually.