< Masalimo 74 >

1 Ndakatulo ya Asafu. Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu? Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?
[A Psalm] of instruction for Asaph. Wherefore hast thou rejected [us], O God, for ever? [wherefore] is thy wrath kindled against the sheep of thy pasture?
2 Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale, fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola, phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.
Remember thy congregation which thou hast purchased from the beginning; thou didst ransom the rod of thine inheritance; this mount Sion wherein thou hast dwelt.
3 Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.
Lift up thine hands against their pride continually; [because of] all that the enemy has done wickedly in thy holy places.
4 Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe; anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.
And they that hate thee have boasted in the midst of thy feast; they have set up their standards for signs,
5 Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo kuti adule mitengo mʼnkhalango.
ignorantly as it were in the entrance above;
6 Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo zonse zimene tinapachika.
they cut down its doors at once with axes as in a wood of trees; they have broken it down with hatchet and stone cutter.
7 Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi; anadetsa malo okhalamo dzina lanu.
They have burnt thy sanctuary with fire to the ground; they have profaned the habitation of thy name.
8 Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.” Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.
They have said in their heart, [even] all their kindred together, Come, let us abolish the feasts of the Lord from the earth.
9 Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa; palibe aneneri amene atsala ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.
We have not seen our signs; there is no longer a prophet; and [God] will not know us any more.
10 Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu? Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?
How long, O God, shall the enemy reproach? shall the enemy provoke thy name forever?
11 Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja? Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!
Wherefore turnest thou away thine hand, and thy right hand from the midst of thy bosom for ever?
12 Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale; Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.
But God is our King of old; he has wrought salvation in the midst of the earth.
13 Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu; munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.
Thou didst establish the sea, in thy might, thou didst break to pieces the heads of the dragons in the water.
14 Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.
Thou didst break to pieces the heads of the dragon; thou didst give him [for] meat to the Ethiopian nations.
15 Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje, munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.
Thou didst cleave fountains and torrents; thou driedst up mighty rivers.
16 Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso; Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.
The day is thine, and the night is thine; thou hast prepared the sun and the moon.
17 Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi; munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.
Thou hast made all the borders of the earth; thou hast made summer and spring.
18 Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova, momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.
Remember this thy creation: an enemy has reproached the Lord, and a foolish people has provoked thy name.
19 Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo; nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.
Deliver not to the wild beasts a soul that gives praise to thee: forget not for ever the souls of thy poor.
20 Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.
Look upon thy covenant: for the dark [places] of the earth are filled with the habitations of iniquity.
21 Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi; osauka ndi osowa atamande dzina lanu.
let not the afflicted and shamed one be rejected: the poor and needy shall praise thy name.
22 Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu; kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.
Arise, O God, plead thy cause: remember thy reproaches that come from the foolish one all the day.
23 Musalekerere phokoso la otsutsana nanu, chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.
Forget not the voice of thy suppliants: let the pride of them that hate thee continually ascend before thee.

< Masalimo 74 >