< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
Asaf'ın mezmuru Tanrı gerçekten İsrail'e, Yüreği temiz olanlara karşı iyidir.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
Ama benim ayaklarım neredeyse tökezlemiş, Adımlarım az kalsın kaymıştı.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
Çünkü kötülerin gönencini gördükçe, Küstahları kıskanıyordum.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
Onlar acı nedir bilmezler, Bedenleri sağlıklı ve semizdir.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
Başkalarının derdini bilmez, Onlar gibi çile çekmezler.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Bu yüzden gurur onların gerdanlığı, Zorbalık onları örten bir giysi gibidir.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Şişmanlıktan gözleri dışarı fırlar, İçleri kötülük kazanı gibi kaynar.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
İnsanlarla eğlenir, kötü niyetle konuşur, Tepeden bakar, baskıyla tehdit ederler.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
Göklere karşı ağızlarını açarlar, Boş sözleri yeryüzünü dolaşır.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Bu yüzden halk onlardan yana döner, Sözlerini ağzı açık dinler.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
Derler ki, “Tanrı nasıl bilir? Bilgisi var mı Yüceler Yücesi'nin?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
İşte böyledir kötüler, Hep tasasız, sürekli varlıklarını artırırlar.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
Anlaşılan boş yere yüreğimi temiz tutmuşum, Ellerimi yıkamışım suçsuzum diye.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
Gün boyu içim içimi yiyor, Her sabah azap çekiyorum.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
“Ben de onlar gibi konuşayım” deseydim, Senin çocuklarına ihanet etmiş olurdum.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
Bunu anlamak için düşündüğümde, Zor geldi bana,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
Tanrı'nın Tapınağı'na girene dek; O zaman anladım sonlarının ne olacağını.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Gerçekten onları kaygan yere koyuyor, Yıkıma sürüklüyorsun.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
Nasıl da bir anda yok oluyor, Siliniveriyorlar dehşet içinde!
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
Uyanan birisi için rüya nasılsa, Sen de uyanınca, ya Rab, Hor göreceksin onların görüntüsünü.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
Kalbim kırıldığında, İçim acı dolduğunda,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
Akılsız ve bilgisizdim, Karşında bir hayvan gibi.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Yine de sürekli seninleyim, Sağ elimden tutarsın beni.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Öğütlerinle yol gösterir, Beni sonunda yüceliğe eriştirirsin.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Senden başka kimim var göklerde? İstemem senden başkasını yeryüzünde.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
Bedenim ve yüreğim tükenebilir, Ama Tanrı yüreğimde güç, Bana düşen paydır sonsuza dek.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
Kuşkusuz yok olacak senden uzak duranlar, Ortadan kaldıracaksın sana vefasızlık edenleri.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
Ama benim için en iyisi Tanrı'ya yakın olmaktır; Bütün işlerini duyurayım diye Sığınak yaptım Egemen RAB'bi kendime.

< Masalimo 73 >