< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
مزمور آساف هرآینه خدا برای اسرائیل نیکوست، یعنی برای آنانی که پاک دل هستند.۱
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
واما من نزدیک بود که پایهایم از راه در رود ونزدیک بود که قدمهایم بلغزد.۲
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
زیرا بر متکبران حسد بردم چون سلامتی شریران را دیدم.۳
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
زیراکه در موت ایشان قیدها نیست و قوت ایشان مستحکم است.۴
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
مثل مردم در زحمت نیستند ومثل آدمیان مبتلا نمی باشند.۵
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
بنابراین گردن ایشان به تکبر آراسته است وظلم مثل لباس ایشان را می‌پوشاند.۶
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
چشمان ایشان از فربهی بدر‌آمده است و از خیالات دل خود تجاوز می‌کنند.۷
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
استهزا می‌کنند و حرفهای بد می‌زنند و سخنان ظلم آمیز را از جای بلندمی گویند.۸
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
دهان خود را بر آسمانها گذارده‌اند وزبان ایشان در جهان گردش می‌کند.۹
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
پس قوم او بدینجا برمی گردند و آبهای فراوان، بدیشان نوشانیده می‌شود.۱۰
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
و ایشان می‌گویند: «خدا چگونه بداند و آیا حضرت اعلی علم دارد؟»۱۱
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
اینک اینان شریر هستند که همیشه مطمئن بوده، در دولتمندی افزوده می‌شوند.۱۲
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
یقین من دل خود را عبث طاهر ساخته و دستهای خود رابه پاکی شسته‌ام.۱۳
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
و من تمامی روز مبتلامی شوم و تادیب من هر بامداد حاضر است.۱۴
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
اگر می‌گفتم که چنین سخن گویم، هر آینه برطبقه فرزندان تو خیانت می‌کردم.۱۵
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
چون تفکرکردم که این را بفهمم، در نظر من دشوار آمد.۱۶
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
تابه قدسهای خدا داخل شدم. آنگاه در آخرت ایشان تامل کردم.۱۷
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
هر آینه ایشان را در جایهای لغزنده گذارده‌ای. ایشان را به خرابیها خواهی انداخت.۱۸
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
چگونه بغته به هلاکت رسیده‌اند! تباه شده، از ترسهای هولناک نیست گردیده‌اند.۱۹
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
مثل خواب کسی چون بیدار شد، ای خداوندهمچنین چون برخیزی، صورت ایشان را ناچیزخواهی شمرد.۲۰
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
لیکن دل من تلخ شده بود و در اندرون خود، دل ریش شده بودم.۲۱
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
و من وحشی بودم ومعرفت نداشتم و مثل بهایم نزد تو گردیدم.۲۲
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
ولی من دائم با تو هستم. تو دست راست مراتایید کرده‌ای.۲۳
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
موافق رای خود مرا هدایت خواهی نمود و بعد از این مرا به جلال خواهی رسانید.۲۴
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
کیست برای من در آسمان؟ و غیر ازتو هیچ‌چیز را در زمین نمی خواهم.۲۵
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
اگرچه جسد و دل من زائل گردد، لیکن صخره دلم وحصه من خداست تا ابدالاباد.۲۶
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
زیرا آنانی که ازتو دورند هلاک خواهند شد. و آنانی را که از توزنا می‌کنند، نابود خواهی ساخت.۲۷
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
و اما مرانیکوست که به خدا تقرب جویم. بر خداوندیهوه توکل کرده‌ام تا همه کارهای تو را بیان کنم.۲۸

< Masalimo 73 >