< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
Ihubo lika-Asafi. Ngempela uNkulunkulu ulungile ku-Israyeli, kulabo abahlanzekileyo enhliziyweni.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
Kodwa mina, inyawo zami zaphose zatshelela; ngaphose ngakhuthisa ukunyathela.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
Ngasuka ngahawukela abaklolodayo ngibona ukuphumelela kwezigangi.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
Kabalazo inhlungu; imizimba yabo iphilile iqinile.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
Kabalayo imithwalo enzima ejayelekileyo ebantwini; kabahlukuluzwa loba yini njengabanye abantu.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Ngakho-ke ukuziqhenya kuyisigqizo sabo entanyeni; bazigqokisa ngokwenza isihluku.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Ezinhliziyweni zabo ezingelazwelo kuphuma ububi; iminakano emibi yezingqondo zabo ayilamikhawulo.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
Bayakloloda, bakhulume ngomona; bayaqholoza basongele ukuncindezela.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
Imilomo yabo ithi izulu selingelabo, lezilimi zabo zihle ziwuthathe umhlaba.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Yikho abantu bakibo bebakholwa, bawanathe amanzi kakhulukazi.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
Bathi, “UNkulunkulu angakwazi kanjani? OPhezukonke ulalo ulwazi na?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Yikho lokhu abayikho khona ababi bavele kabananzi, iyanda eyabo inotho.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
Ngempela bekuyize ukugcina inhliziyo yami ihlanzekile; kube yize ukugeza izandla zami ngokungelacala.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
Ilanga lonke ngitshona ngikhathazwa; ngiyajeziswa ekuseni zonke insuku.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
Aluba ngangithe, “Ngizakhuluma ngitsho njalo,” ngabe ngangibakhohlisa abantwabakho.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
Ngathi ngizama ukukuzwisisa konke lokhu ngezwa kungisinda,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
ngaze ngangena endlini engcwele kaNkulunkulu; lapho-ke ngasengizwisisa isiphetho sabo.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Ngempela uyababeka endaweni etshelelayo; ubalahlela phansi ekubhujisweni.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
Yeka, ukubhujiswa kwabo lula nje, bakhuculwe nje yikwesaba!
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
Njengephupho nxa umuntu ephaphama kuzakuba njalo lapho usuvuka, Thixo, uzabeyisa njengemifanekiso yengqondo kuphela.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
Lapho inhliziyo yami yayifuthelene lomoya wami uthukuthele,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
ngangiyisithutha esingaziyo; ngangiyinyamazana yeganga kuwe.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Ikanti ngihlezi ngilawe; uyangibamba ngesandla sami sokunene.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Uyangikhokhela ngokweluleka kwakho kuthi ngemva kwalokho uzangithatha ungise ebukhosini.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Ngilobani na ezulwini ngaphandle kwakho? Lomhlaba kawulakho engikufisayo ngaphandle kwakho.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
Inyama yami lenhliziyo yami kungehluleka kodwa uNkulunkulu ungamandla enhliziyo yami, uyisabelo sami laphakade.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
Labo abakhatshana lawe bazabhubha; uyababhidliza bonke abangathembekanga kuwe.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
Kodwa mina kimi kuhle ukuba seduze loNkulunkulu. Sengenze uThixo Wobukhosi isiphephelo sami; ngizafakaza ngazozonke izenzo zakho.

< Masalimo 73 >