< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
מזמור לאסף אך טוב לישראל אלהים-- לברי לבב
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
ואני--כמעט נטוי (נטיו) רגלי כאין שפכה (שפכו) אשרי
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
כי-קנאתי בהוללים שלום רשעים אראה
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
כי אין חרצבות למותם ובריא אולם
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
בעמל אנוש אינמו ועם-אדם לא ינגעו
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
לכן ענקתמו גאוה יעטף-שית חמס למו
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
יצא מחלב עינמו עברו משכיות לבב
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
ימיקו וידברו ברע עשק ממרום ידברו
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
שתו בשמים פיהם ולשונם תהלך בארץ
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
לכן ישיב (ישוב) עמו הלם ומי מלא ימצו למו
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
ואמרו איכה ידע-אל ויש דעה בעליון
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
הנה-אלה רשעים ושלוי עולם השגו-חיל
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
אך-ריק זכיתי לבבי וארחץ בנקיון כפי
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
ואהי נגוע כל-היום ותוכחתי לבקרים
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
אם-אמרתי אספרה כמו הנה דור בניך בגדתי
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
ואחשבה לדעת זאת עמל היא (הוא) בעיני
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
עד-אבוא אל-מקדשי-אל אבינה לאחריתם
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
אך בחלקות תשית למו הפלתם למשואות
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
איך היו לשמה כרגע ספו תמו מן-בלהות
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
כחלום מהקיץ-- אדני בעיר צלמם תבזה
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
כי יתחמץ לבבי וכליותי אשתונן
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
ואני-בער ולא אדע בהמות הייתי עמך
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
ואני תמיד עמך אחזת ביד-ימיני
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
בעצתך תנחני ואחר כבוד תקחני
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
מי-לי בשמים ועמך לא-חפצתי בארץ
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
כלה שארי ולבבי צור-לבבי וחלקי--אלהים לעולם
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
כי-הנה רחקיך יאבדו הצמתה כל-זונה ממך
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
ואני קרבת אלהים-- לי-טוב שתי באדני יהוה מחסי לספר כל-מלאכותיך

< Masalimo 73 >