< Masalimo 73 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
Un psaume d'Asaph. Certes, Dieu est bon pour Israël, à ceux qui ont le cœur pur.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
Mais quant à moi, mes pieds étaient presque partis. Mes pas avaient presque glissé.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
Car j'étais envieux des arrogants, quand j'ai vu la prospérité des méchants.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
Car il n'y a pas de lutte dans leur mort, mais leur force est ferme.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
Ils sont libérés des fardeaux des hommes, ils ne sont pas non plus frappés comme les autres hommes.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
C'est pourquoi l'orgueil est comme un collier à leur cou. La violence les couvre comme un vêtement.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Leurs yeux sont gonflés de graisse. Leur esprit dépasse les limites de la vanité.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
Ils se moquent et parlent avec méchanceté. Dans leur arrogance, ils menacent d'oppression.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
Ils ont placé leur bouche dans les cieux. Leur langue traverse la terre.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
C'est pourquoi leur peuple revient vers eux, et ils boivent des eaux en abondance.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
Ils disent: « Comment Dieu le sait-il? Y a-t-il de la connaissance dans le Très-Haut? »
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Voici, ce sont les méchants. Étant toujours à l'aise, ils augmentent leurs richesses.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
C'est en vain que j'ai purifié mon cœur, et je me suis lavé les mains en toute innocence,
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
Car toute la journée, j'ai été tourmenté, et puni chaque matin.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
Si j'avais dit: « Je vais parler ainsi », Voici, j'aurais trahi la génération de vos enfants.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
Quand j'ai essayé de comprendre ça, c'était trop douloureux pour moi...
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
jusqu'à ce que j'entre dans le sanctuaire de Dieu, et envisagé leur fin.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Tu les as placés dans des endroits glissants. Vous les jetez à la destruction.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
Comme ils sont soudainement détruits! Ils sont complètement emportés par la terreur.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
Comme un rêve quand on se réveille, alors, Seigneur, à votre réveil, vous mépriserez leurs fantasmes.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
Car mon âme était affligée. J'étais aigri dans mon cœur.
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
J'étais tellement insensé et ignorant. J'étais une bête brute avant toi.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Néanmoins, je suis continuellement avec vous. Tu as tenu ma main droite.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Tu me guideras par tes conseils, et ensuite me recevoir dans la gloire.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Qui ai-je dans le ciel? Il n'y a personne sur terre que je désire en dehors de toi.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
Ma chair et mon cœur sont défaillants, mais Dieu est la force de mon cœur et mon partage pour toujours.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
Car voici, ceux qui sont loin de toi périront. Tu as détruit tous ceux qui t'étaient infidèles.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
Mais il est bon pour moi de m'approcher de Dieu. J'ai fait du Seigneur Yahvé mon refuge, pour que je puisse raconter toutes tes œuvres.