< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
`The salm of Asaph. God of Israel is ful good; to hem that ben of riytful herte.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
But my feet weren moued almeest; my steppis weren sched out almeest.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
For Y louede feruentli on wickid men; seynge the pees of synneris.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
For biholdyng is not to the deth of hem; and stidefastnesse in the sikenesse of hem.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
Thei ben not in the trauel of men; and thei schulen not be betun with men.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Therfore pride helde hem; thei weren hilid with her wickidnesse and vnfeithfulnesse.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
The wickidnesse of hem cam forth as of fatnesse; thei yeden in to desire of herte.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
Thei thouyten and spaken weiwardnesse; thei spaken wickidnesse an hiy.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
Thei puttiden her mouth in to heuene; and her tunge passide in erthe.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Therfor my puple schal be conuertid here; and fulle daies schulen be foundun in hem.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
And thei seiden, How woot God; and whether kunnyng is an heiye, `that is, in heuene?
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Lo! thilke synneris and hauynge aboundance in the world; helden richessis.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
And Y seide, Therfor without cause Y iustifiede myn herte; and waischide myn hoondis among innocentis.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
And Y was betun al dai; and my chastisyng was in morutidis.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If Y seide, Y schal telle thus; lo! Y repreuede the nacioun of thi sones.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
I gesside, that Y schulde knowe this; trauel is bifore me.
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
Til Y entre in to the seyntuarie of God; and vndurstonde in the last thingis of hem.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Netheles for gilis thou hast put to hem; thou castidist hem doun, while thei weren reisid.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
Hou ben thei maad into desolacioun; thei failiden sodeynli, thei perischiden for her wickidnesse.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
As the dreem of men that risen; Lord, thou schalt dryue her ymage to nouyt in thi citee.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
For myn herte is enflaumed, and my reynes ben chaungid;
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
and Y am dryuun to nouyt, and Y wiste not.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
As a werk beeste Y am maad at thee; and Y am euere with thee.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Thou heldist my riythond, and in thi wille thou leddist me forth; and with glorie thou tokist me vp.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
For whi what is to me in heuene; and what wolde Y of thee on erthe?
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
Mi fleische and myn herte failide; God of myn herte, and my part is God withouten ende.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
For lo! thei that drawen awei fer hem silf fro thee, `bi deedli synne, schulen perische; thou hast lost alle men that doen fornycacioun fro thee.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
But it is good to me to cleue to God; and to sette myn hope in the Lord God. That Y telle alle thi prechyngis; in the yatis of the douyter of Syon.

< Masalimo 73 >