< Masalimo 73 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
melody to/for Asaph surely pleasant to/for Israel God to/for pure heart
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
and I like/as little (to stretch *Q(K)*) foot my like/as nothing (to pour: scatter *Q(K)*) step my
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
for be jealous in/on/with to be foolish peace: well-being wicked to see: see
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
for nothing bond to/for death their and fat strength their
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
in/on/with trouble human nothing they and with man not to touch
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
to/for so to ornament them pride to envelope garment violence to/for them
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
to come out: come from fat eye their to pass figure heart
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
to mock and to speak: speak in/on/with bad: evil oppression from height to speak: speak
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
to appoint in/on/with heaven lip their and tongue their to go: walk in/on/with land: country/planet
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
to/for so (to return: return *Q(K)*) people his here and water full to drain to/for them
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
and to say how? to know God and there knowledge in/on/with Most High
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
behold these wicked and at ease forever: enduring to increase strength: rich
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
surely vain to clean heart my and to wash: wash in/on/with innocence palm my
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
and to be to touch all [the] day and argument my to/for morning
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
if to say to recount like behold generation son: child your to act treacherously
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
and to devise: think [emph?] to/for to know this trouble (he/she/it *Q(K)*) in/on/with eye: appearance my
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
till to come (in): come to(wards) sanctuary God to understand to/for end their
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
surely in/on/with smoothness to set: make to/for them to fall: fall them to/for desolation
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
how? to be to/for horror: destroyed like/as moment to cease to finish from terror
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
like/as dream from to awake Lord in/on/with to rouse image their to despise
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
for to leaven heart my and kidney my to sharpen
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
and I stupid and not to know animal to be with you
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
and I continually with you to grasp in/on/with hand right my
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
in/on/with counsel your to lead me and after glory to take: recieve me
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
who? to/for me in/on/with heaven and with you not to delight in in/on/with land: country/planet
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
to end: expend flesh my and heart my rock heart my and portion my God to/for forever: enduring
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
for behold removed your to perish to destroy all to fornicate from you
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
and I nearness God to/for me pleasant to set: make in/on/with Lord YHWH/God refuge my to/for to recount all work your