< Masalimo 73 >
1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
“BOOK III. A psalm of Asaph.” Truly God is good to Israel, —To those who are pure in heart.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
Yet my feet almost gave way; My steps had well nigh slipped:
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
For I was envious of the proud, When I saw the prosperity of the wicked.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
For they have no pains even to their death; Their bodies are in full health.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
They have not the woes of other men, Neither are they smitten like other men.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Therefore pride encircleth their neck as a collar; Violence covereth them as a garment.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
From their bosom issueth their iniquity; The designs of their hearts burst forth.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
They mock, and speak of malicious oppression; Their words are haughty;
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
They stretch forth their mouth to the heavens, And their tongue goeth through the earth;
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Therefore his people walk in their ways, And there drink from full fountains.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
And they say, “How doth God know? How can there be knowledge with the Most High?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Behold these are the ungodly! Yet they are ever prosperous; they heap up riches.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
Verily I have cleansed my heart in vain; In vain have I washed my hands in innocence.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
For every day have I been smitten; Every morn have I been chastened.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If I should resolve to speak like them, Surely I should be treacherous to the family of thy children.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
So, when I studied to know this, It was painful to my eyes;
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
Until I went into the sanctuaries of God, And considered what was their end.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Behold! thou hast set them on slippery places; Thou castest them down into unseen pits.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
How are they brought to desolation in a moment, And utterly consumed with sudden destruction!
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
As a dream when one awaketh, Thou, O Lord! when thou awakest, wilt make their vain show a derision.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
When my heart was vexed And I was pierced in my reins,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
Then was I stupid and without understanding; I was like one of the brutes before thee.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Yet am I ever under thy care; By my right hand thou dost hold me up.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Thou wilt guide me with thy counsel, And at last receive me in glory.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Whom have I in heaven but thee, And whom on earth do I love in comparison with thee?
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
Though my flesh and my heart fail, God is the strength of my heart, and my portion for ever.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
For, lo! they who are far from thee perish; Thou destroyest all who estrange themselves from thee.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
But it is good for me to draw near to God; I put my trust in the Lord Jehovah, That I may declare all thy works.