< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
A PSALM OF ASAPH. Surely God [is] good to Israel, to the clean of heart. And I—as a little thing, My feet have been turned aside,
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
As nothing, my steps have slipped, For I have been envious of the boastful,
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
I see the peace of the wicked, That there are no bands at their death,
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
And their might [is] firm.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
They are not in the misery of mortals, And they are not plagued with common men.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Therefore pride has encircled them, Violence covers them as a dress.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Their eye has come out from fat. The imaginations of the heart transgressed;
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
They do corruptly, And they speak in the wickedness of oppression, They speak from on high.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
They have set their mouth in the heavens, And their tongue walks in the earth.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Therefore His people return here, And waters of fullness are wrung out to them.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
And they have said, “How has God known? And is there knowledge in the Most High?”
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Behold, these [are] the wicked and easy ones of the age, They have increased strength.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
Only—a vain thing! I have purified my heart, And I wash my hands in innocence,
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
And I am plagued all the day, And my reproof—every morning.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If I have said, “I recount thus,” Behold, I have deceived a generation of Your sons.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
And I think to know this, It [is] perverseness in my eyes,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
Until I come into the sanctuaries of God, I attend to their latter end.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Surely You set them in slippery places, You have caused them to fall to desolations.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
How they have become a desolation as in a moment, They have been ended—consumed from terrors.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
As a dream from awakening, O Lord, In awaking, You despise their image.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
For my heart shows itself violent, And my reins prick themselves,
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
And I am brutish, and do not know. I have been a beast with You.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
And I [am] continually with You, You have laid hold on my right hand.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
You lead me with Your counsel, And after, receive me [to] glory.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Whom do I have in the heavens? And none have I desired in earth [besides] You.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
My flesh and my heart have been consumed, God [is] the rock of my heart and my portion for all time.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
For behold, those far from You perish, You have cut off everyone, Who is going whoring from You.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
And [the] nearness of God to me [is] good, I have placed my refuge in Lord YHWH, To recount all Your works!

< Masalimo 73 >