< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
A psalm of Asaph. Truly God is good to Israel, to those whose minds are pure.
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
But I was stumbling, my feet were starting to slide,
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
because I was jealous of self-important people—I saw how well the wicked were doing.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
They don't ever seem to get sick; they are strong and healthy.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
They don't have problems like other people; they don't get hit by disasters like everybody else.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
They wear their pride like a necklace; they clothe themselves with violence.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Their eyes bulge out because they're so fat; their minds are full of selfish vanity.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
They mock people, and speak maliciously; they arrogantly threaten cruelty.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
They talk irreverently against heaven above, and defame people here on earth.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
As a result people turn to them and drink in everything they say.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
“God won't find out,” they say. “The Most High doesn't even know what's going on!”
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Look at these wicked people! They don't have a care in the world, and they're always making money!
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
It's been pointless to keep my mind pure and my hands clean.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
I'm cursed with suffering all day long; every morning I'm punished.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If I'd talked like this to others, I would have betrayed your people.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
So I thought about it and tried to understand, but it looked like a lot of hard work to me—
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
until I went into God's Temple. Then I understood what happens to the wicked in the end.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
For you send them on a slippery path; you throw them down to destruction.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
How quickly they're destroyed! They come to a terrifying end.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
Like waking up from a dream, Lord—when you get up you will forget all about them!
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
At that time my thoughts were bitter. I felt like I had been stabbed.
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
I was stupid and ignorant. I was like a brute beast to you.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Yet I'm always with you; you hold me by the hand.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
You tell me what to do; and ultimately you will welcome me in glory.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
Who is there in heaven for me except you? And I want nothing on earth except you.
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
My body and my mind may fail, but God is the foundation of my life. He is mine forever!
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
Those people who are far from God will die. You destroy all those unfaithful to you.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
But I love to stay close to God! I have chosen the Lord God to protect me. I will share all that you have done.

< Masalimo 73 >