< Masalimo 73 >

1 Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
A Psalm for Asaph. How good is God to Israel, to the upright in heart!
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
But my feet were almost overthrown; my goings very nearly slipped.
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
For I was jealous of the transgressors, beholding the tranquility of sinners.
4 Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
For there is no sign of reluctance in their death: and [they have] firmness under their affliction.
5 Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
They are not in the troubles of [other] men; and they shall not be scourged with [other] men.
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
Therefore pride has possessed them; they have clothed themselves with their injustice and ungodliness.
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
Their injustice shall go forth as out of fatness: they have fulfilled their intention.
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
They have taken counsel and spoken in wickedness: they have uttered unrighteousness loftily.
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
They have set their mouth against heaven, and their tongue has gone through upon the earth.
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
Therefore shall my people return hither: and full days shall be found with them.
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
And they said, How does God know? and is there knowledge in the Most High?
12 Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
Behold, these [are] the sinners, and they that prosper always: they have possessed wealth.
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
And I said, Verily in vain have I justified my heart, and washed my hands in innocency.
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
For I was plagued all the day, and my reproof [was] every morning.
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
If I said, I will speak thus; behold, I [should] have broken covenant with the generation of thy children.
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
And I undertook to understand this, [but] it is too hard for me,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
until I go into the sanctuary of God; [and so] understand the latter end.
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
Surely thou hast appointed [judgments] to them because of their crafty dealings: thou hast cast them down when they were lifted up.
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
How have they become desolate! suddenly they have failed: they have perished because of their iniquity.
20 Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
As the dream of one awakening, O Lord, in thy city thou wilt despise their image.
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
For my heart has rejoiced, and my reins have been gladdened.
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
But I [was] vile and knew not: I became brutish before thee.
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
Yet I am continually with thee: thou hast holden my right hand.
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
Thou hast guided me by thy counsel, and thou hast taken me to thyself with glory.
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
For what have I in heaven [but thee]? and what have I desired upon the earth beside thee?
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
My heart and my flesh have failed: [but] God [is the strength] of my heart, and God is my portion for ever.
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
For, behold, they that remove themselves far from thee shall perish: thou hast destroyed every one that goes a whoring from thee.
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.
But it is good for me to cleave close to God, to put my trust in the Lord; that I may proclaim all thy praises in the gates of the daughter of Sion.

< Masalimo 73 >