< Masalimo 72 >
1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Про Соломона. Боже, даруй Твоє правосуддя цареві і праведність Твою – синові царя.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Нехай судить він народ Твій справедливо й страдників Твоїх – чесно.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Нехай гори принесуть народові мир, а пагорби – праведність.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Нехай судить він пригнічених народу, врятує дітей бідняків і вразить гнобителя.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Будуть боятися Тебе, аж поки сонце і місяць існують, із роду в рід.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Нехай зійде він як дощ на покіс, як рясний дощ, що зрошує землю.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
У дні його нехай процвітає праведник і мир великий не припиняється, аж поки місяць не згасне.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Він пануватиме від моря й до моря і від ріки аж до країв землі.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Схилять перед ним коліна мешканці пустель, і вороги його лизатимуть пил.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Царі Таршишу й віддалених берегів платитимуть йому данину, царі Шеви і Севи піднесуть дари [на знак покори].
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
І вклоняться йому всі царі, усі народи служитимуть йому.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Бо врятує він бідного, коли той волатиме, і пригніченого, у якого немає помічника.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Він милість виявить убогому й бідняку і врятує душі злидарів.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
Викупить душі їхні з-під влади насильства, адже кров їхня буде дорогоцінна в очах його.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Нехай він живе [довго], і нехай дано йому буде золото Шеви. Нехай моляться за нього завжди, нехай цілий день благословляють його!
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Нехай пшениці буде вдосталь на землі; на вершинах пагорбів нехай коливається колосся, немов на Лівані, і люд рясніє в містах, немов трава на землі.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Нехай ім’я його перебуває вічно, аж поки існує сонце. Через нього благословенними будуть усі народи; вони вважатимуть його тим, що щастя приносить.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Благословенний Господь, Бог Ізраїля, Який один лиш творить чудеса!
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Благословенне ім’я слави Його повік, і вся земля наповниться Його славою!
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Завершилися молитви Давида, сина Єссеєвого.