< Masalimo 72 >
1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Av Salomo. Gud, giv åt konungen dina rätter och din rättfärdighet åt konungasonen.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Han döme ditt folk med rättfärdighet och dina betryckta med rätt.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Bergen bäre frid åt folket, så ock höjderna, genom rättfärdighet.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Han skaffe rätt åt de betryckta i folket, han frälse de fattiga och krosse förtryckaren.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Dig frukte man, så länge solen varar, och så länge månen skiner, från släkte till släkte.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Han vare lik regnet som faller på ängen, lik en regnskur som vattnar jorden.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
I hans dagar blomstre den rättfärdige, och stor frid råde, till dess ingen måne mer finnes.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Må han härska från hav till hav och ifrån floden intill jordens ändar.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
För honom buge sig öknens inbyggare, och hans fiender slicke stoftet.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Konungarna från Tarsis och havsländerna hembäre skänker, konungarna av Saba och Seba bäre fram gåvor.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
Ja, alla konungar falle ned för honom, alla hedningar tjäne honom.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Ty han skall rädda den fattige som ropar och den betryckte och den som ingen hjälpare har.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Han skall vara mild mot den arme och fattige; de fattigas själar skall han frälsa.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
Ifrån förtryck och våld skall han förlossa deras själ, och deras blod skall aktas dyrt i hans ögon.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Må han leva; må man föra till honom guld från Saba. Ständigt bedje man för honom, alltid välsigne man honom.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Ymnigt växe säden i landet, ända till bergens topp; dess frukt må susa likasom Libanons skog; och folk blomstre upp i städerna såsom örter på marken.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Hans namn förblive evinnerligen; så länge solen skiner, fortplante sig hans namn. Och i honom välsigne man sig; alla hedningar prise honom säll.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Lovad vare HERREN Gud, Israels Gud, som allena gör under!
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Och lovat vare hans härliga namn evinnerligen, och hela jorden vare full av hans ära! Amen, Amen.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Slut på Davids, Isais sons, böner. Tredje boken