< Masalimo 72 >

1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Daj kralju svoje sodbe, oh Bog in svojo pravičnost kraljevemu sinu.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Tvoje ljudstvo bo sodil s pravičnostjo in tvoje uboge s sodbo.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Gore bodo ljudstvu prinesle mir in majhni hribi po pravičnosti.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Sodil bo uboge izmed ljudstva, rešil bo otroke pomoči potrebnih, zatiralca pa bo razbil na koščke.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Bali se te bodo, dokler ostajata sonce in luna, skozi vse rodove.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Prišel bo dol kakor dež na pokošeno travo, kakor nalivi, ki namakajo zemljo.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
V njegovih dneh bo pravični cvetel in obilje miru tako dolgo, kot ostaja luna.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Imel bo tudi gospostvo od morja do morja in od reke do koncev zemlje.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Tisti, ki prebivajo v divjini, se bodo poklonili pred njim, njegovi sovražniki pa bodo lizali prah.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Kralji iz Taršíša in z otokov bodo prinašali darila. Kralji iz Sabe in Sebe bodo ponujali darove.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
Da, vsi kralji bodo padli dol pred njim. Služili mu bodo vsi narodi.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Kajti osvobodil bo pomoči potrebnega, ko vpije; tudi ubogega in tistega, ki nima pomočnika.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Prizanesel bo ubogemu in pomoči potrebnemu in rešil duše pomoči potrebnih.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
Njihove duše bo odkupil pred prevaro in nasiljem, in njihova kri bo dragocena v njegovem pogledu.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Živel bo in njemu bo dano od zlata iz Sabe. Zanj bo narejena tudi nenehna molitev in dnevno bo hvaljen.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Prgišče žita bo na zemlji do vrhov gorá. Njen sad se bo tresel kakor Libanon in tisti iz mesta bodo cveteli kakor zemeljska trava.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Njegovo ime bo ostalo na veke. Njegovo ime se bo razširjalo, dokler [bo] sonce in ljudje bodo blagoslovljeni v njem. Vsi narodi ga bodo imenovali blagoslovljen.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Blagoslovljen bodi Gospod Bog, Izraelov Bog, ki edini dela čudovite stvari.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Blagoslovljeno bodi njegovo veličastno ime na veke in vsa zemlja naj bo napolnjena z njegovo slavo. Amen in Amen.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Molitve Davida, Jesejevega sina, so končane.

< Masalimo 72 >