< Masalimo 72 >

1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Боже, суд Твой цареви даждь, и правду Твою сыну цареву:
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
судити людем Твоим в правде и нищым Твоим в суде.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Да восприимут горы мир людем и холми правду.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Судит нищым людским, и спасет сыны убогих, и смирит клеветника.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
И пребудет с солнцем, и прежде луны рода родов.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Снидет яко дождь на руно, и яко капля каплющая на землю.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
Возсияет во днех его правда и множество мира, дондеже отимется луна.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
И обладает от моря до моря, и от рек до конец вселенныя.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Пред ним припадут Ефиопляне, и врази его персть полижут.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Царие Фарсийстии и острови дары принесут, царие Аравстии и Сава дары приведут:
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
и поклонятся ему вси царие земстии, вси языцы поработают ему.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Яко избави нища от сильна, и убога, емуже не бе помощника.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Пощадит нища и убога, и душы убогих спасет:
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
от лихвы и от неправды избавит душы их, и честно имя его пред ними.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
И жив будет, и дастся ему от злата Аравийска: и помолятся о нем выну, весь день благословят его.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Будет утверждение на земли на версех гор: превознесется паче Ливана плод его, и процветут от града яко трава земная.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Будет имя его благословено во веки, прежде солнца пребывает имя его: и благословятся в нем вся колена земная, вси языцы ублажат его.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Благословен Господь Бог Израилев, творяй чудеса един,
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
и благословено имя славы Его во век и в век века: и исполнится славы Его вся земля: буди, буди.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Masalimo 72 >