< Masalimo 72 >

1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Думнезеуле, дэ жудекэциле Тале ымпэратулуй ши дэ дрептатя Та фиулуй ымпэратулуй!
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Ши ел ва жудека пе попорул Тэу ку дрептате ши пе ненорочиций Тэй ку непэртинире.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
Мунций вор адуче паче попорулуй ши дялуриле, де асеменя, ка урмаре а дрептэций Тале.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Ел ва фаче дрептате ненорочицилор попорулуй, ва скэпа пе копиий сэракулуй ши ва здроби пе асупритор.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Аша кэ се вор теме де Тине кыт ва фи соареле ши кыт се ва арэта луна, дин ням ын ням;
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
ва фи ка о плоае каре каде пе ун пэмынт косит, ка о плоае репеде каре удэ кымпия.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
Ын зилеле луй ва ынфлори чел неприхэнит ши ва фи белшуг де паче пынэ ну ва май фи лунэ.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Ел ва стэпыни де ла о маре ла алта ши де ла рыу пынэ ла марӂиниле пэмынтулуй.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Локуиторий пустиулуй ышь вор плека ӂенункюл ынаинтя луй ши врэжмаший вор линӂе цэрына.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
Ымпэраций Тарсисулуй ши ай остроавелор вор плэти бирурь, ымпэраций Себей ши Сабей вор адуче дарурь.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
Да, тоць ымпэраций се вор ынкина ынаинтя луй, тоате нямуриле ый вор служи.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Кэч ел ва избэви пе сэракул каре стригэ ши пе ненорочитул каре н-аре ажутор.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Ва авя милэ де чел ненорочит ши де чел липсит ши ва скэпа вяца сэрачилор;
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
ый ва избэви де апэсаре ши де силэ ши сынӂеле лор ва фи скумп ынаинтя луй.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Ей вор трэи ши-й вор да аур дин Себа; се вор руга неынчетат пентру ел ши-л вор бинекувынта ын фиекаре зи.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Ва фи белшуг де грыу ын царэ пынэ ын вырфул мунцилор ши спичеле лор се вор клэтина ка ши копачий дин Либан; оамений вор ынфлори ын четэць ка ярба пэмынтулуй.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Нумеле луй ва дэйнуи пе вечие: кыт соареле ый ва цине нумеле. Ку ел се вор бинекувынта уний пе алций, ши тоате нямуриле ыл вор нуми феричит.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Бинекувынтат сэ фие Домнул Думнезеул луй Исраел, сингурул каре фаче минунь!
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Бинекувынтат сэ фие ын вечь слэвитул Луй Нуме! Тот пэмынтул сэ се умпле де слава Луй! Амин! Амин!
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Сфыршитул ругэчунилор луй Давид, фиул луй Исай.

< Masalimo 72 >