< Masalimo 72 >
1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Per Salomone O DIO, da' i tuoi giudicii al re, E la tua giustizia al figliuolo del re.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
Ed egli giudicherà il tuo popolo in giustizia, Ed i tuoi poveri afflitti in dirittura.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
I monti produrranno pace al popolo; E i colli [saranno pieni] di giustizia.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
Egli farà ragione a' poveri afflitti d'infra il popolo; Egli salverà i figliuoli del misero, E fiaccherà l'oppressore.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
Essi ti temeranno per ogni età, Mentre dureranno il sole e la luna.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
Egli scenderà come pioggia sopra erba segata; Come pioggia minuta che adacqua la terra.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
Il giusto fiorirà a' dì d'esso, E [vi sarà] abbondanza di pace, finchè non [vi sia] più luna.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Ed egli signoreggerà da un mare all'altro, E dal fiume fino alle estremità della terra.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Quelli che abitano ne' deserti s'inchineranno davanti a lui, Ed i suoi nemici leccheranno la polvere.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
I re di Tarsis e delle isole [gli] pagheranno tributo; I re di Etiopia e di Arabia [gli] porteranno doni.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
E tutti i re l'adoreranno, Tutte le nazioni gli serviranno.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
Perciocchè egli libererà il bisognoso che grida, E il povero afflitto, e [colui che] non [ha] alcuno che lo aiuti.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
Egli avrà compassione del misero e del bisognoso, E salverà le persone de' poveri.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
Egli riscoterà la vita loro da frode e da violenza; E il sangue loro sarà prezioso davanti a lui.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Così egli viverà, ed [altri] gli darà dell'oro di Etiopia; E pregherà per lui del continuo, e tuttodì lo benedirà.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
Essendo seminata in terra, sulla sommità de' monti, pure una menata di frumento, Quello ch'essa produrrà farà romore come il Libano; E [gli abitanti] delle città fioriranno come l'erba della terra.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
Il suo nome durerà in eterno, Il suo nome sarà perpetuato di generazione in generazione, Mentre vi sarà sole; E tutte le nazioni saranno benedette in lui, [E] lo celebreranno beato.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Benedetto [sia] il Signore Iddio, l'Iddio d'Israele, Il qual solo fa maraviglie.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
Benedetto [sia] ancora eternamente il Nome suo glorioso; E sia tutta la terra ripiena della sua gloria. Amen, Amen.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
[Qui] finiscono le orazioni di Davide, figliuolo d'Isai.