< Masalimo 72 >
1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
E HAAWI i kou mau kanawai i ke alii, e ke Akua, A i kau pono hoi i ke keiki a ke alii.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
E hooponopono oia i kou poe kanaka ma ka pololei. A i kou poe haahaa ma ka pono.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
A e halihali mai no na mauna i ka pomaikai i kanaka, A me na puu liilii hoi, ma ka pono.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
E hooponopono oia i ka poe kaumaha o na kanaka, E hoola oia i na keiki a ka poe ilihune, E hana pepe i ka mea hooluhihewa.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
E weliweli mau lakou ia oe i ka wa o ka la, A i ka luli ana o ka mahina, i na hanauna a pau.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
E iho mai no ia e like me ka ua maluna o ka aina mauu i okiia; Me na kulu ua hoi i hoopulu iho i ka honua.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
E mohala ae ka poe pono i kona mau la, A me ka pomaikai nui a e ole loa ka mahina.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
E hoomalu aupuni oia mai ke kai a i ke kai, A mai ka muliwai hoi a i na welelau o ka honua.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
A imua o kona alo e kulou iho ai ko ka waonahele; A e palu no hoi kona poe enemi i ka lepo.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
E halihali mai na'lii o Taresisa a o na mokupuni i na makana; A e haawi mai no hoi na'lii o Seheba a me Seba i ko lakou mau haawina.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
Oia, e moe iho hoi na'lii a pau imua o kona alo; E pau hoi na lahuikanaka i ka malama ia ia.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
No ka mea, hoopakele no oia i ka mea waiwai ole i kona kahea ana; I ka mea ilihune hoi, a me ka mea nele i ke kokua ole.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
E hookoe mai no oia i ka mea haahaa, a me ka nele, A e hoola hoi i na uhane o ka poe hemahema.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
E hoopakele oia i ko lakou uhane i ka wahahee a me ka lalau wale: A he mea minamina ko lakou koko i kona mau maka.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
E ola no ia, a e haawiia nona ke gula no Seheba: E mau ana no ka pule nona; A e hoomaikai no ia i kela la i keia la.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
E nui auanei ka palaoa ma ka honua, ma ka piko o na mauna; A e luliluli kona hua e like me Lebanona: A e mohala ae ko ke kulanakauhale me he mauu la o ka honua.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
E mau ana no hoi kona inoa; E ulu no kona inoa, a e ole loa ka la: A e pomaikai na kanaka ia ia: E pau hoi na lahuikanaka i ke kapa aku ia ia he pomaikai.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
E hoomaikaiia o Iehova ke Akua, ko Iseraela Akua, Ka mea nana wale no i hana na mea kupaianaha.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
E hoonani mau loa ia'ku kona inoa ihi, E hoopaapuia ka honua a pau i kona nani; Amene, a Amene.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Pau na pule a Davida ke keiki a Iese.